< Psalm 85 >

1 Ein Psalm der Kinder Korah, vorzusingen. HERR, der du bist vormals gnädig gewesen deinem Lande und hast die Gefangenen Jakobs erlöset;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 der du die Missetat vormals vergeben hast deinem Volk und alle ihre Sünde bedecket, (Sela)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 der du vormals hast all deinen Zorn aufgehoben und dich gewendet von dem Grimm deines Zorns;
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 tröste uns, Gott, unser Heiland, und laß ab von deiner Ungnade über uns!
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Willst du denn ewiglich über uns zürnen und deinen Zorn gehen lassen immer für und für?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Willst du uns denn nicht wieder erquicken, daß sich dein Volk über dir freuen möge?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 HERR, erzeige uns deine Gnade und hilf uns!
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Ach, daß ich hören sollte, das Gott der HERR redet, daß er Frieden zusagte seinem Volk und seinen Heiligen, auf daß sie nicht auf eine Torheit geraten!
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Doch ist ja seine Hilfe nahe denen, die ihn fürchten, daß in unserm Lande Ehre wohne;
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 daß Güte und Treue einander begegnen, Gerechtigkeit und Friede sich küssen;
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 daß Treue auf der Erde wachse, und Gerechtigkeit vom Himmel schaue;
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 daß uns auch der HERR Gutes tue, damit unser Land sein Gewächs gebe;
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalm 85 >