< Psalm 76 >

1 Ein Psalmlied Assaphs, auf Saitenspiel vorzusingen. Gott ist in Juda bekannt, in Israel ist sein Name herrlich.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 Zu Salem ist sein Gezelt und seine Wohnung zu Zion.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Daselbst zerbricht er die Pfeile des Bogens, Schild, Schwert und Streit. (Sela)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Du bist herrlicher und mächtiger denn die Raubeberge.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Die Stolzen müssen beraubet werden und entschlafen, und alle Krieger müssen die Hände lassen sinken.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 Von deinem Schelten, Gott Jakobs, sinkt in Schlaf beide Roß und Wagen.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Du bist erschrecklich. Wer kann vor dir stehen, wenn du zürnest?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Wenn du das Urteil lässest hören vom Himmel, so erschrickt das Erdreich und wird still,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 wenn Gott sich aufmacht, zu richten, daß er helfe allen Elenden auf Erden. (Sela)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 Wenn Menschen wider dich wüten, so legest du Ehre ein; und wenn sie noch mehr wüten, bist du auch noch gerüstet.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Gelobet und haltet dem HERRN eurem Gott, alle, die ihr um ihn her seid; bringet Geschenke dem Schrecklichen,
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psalm 76 >