< Psalm 34 >

1 Ein Psalm Davids, da er seine Gebärde verstellete vor Abimelech, der ihn von sich trieb, und er wegging. Ich will den HERRN loben allezeit; sein Lob soll immerdar in meinem Munde sein.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Meine Seele soll sich rühmen des HERRN, daß die Elenden hören und sich freuen.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Preiset mit mir den HERRN und laßt uns miteinander seinen Namen erhöhen!
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Da ich den HERRN suchte, antwortete er mir und errettete mich aus aller meiner Furcht.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Welche ihn ansehen und anlaufen, deren Angesicht wird nicht zuschanden.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Da dieser Elende rief, hörete der HERR und half ihm aus allen seinen Nöten.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Der Engel des HERRN lagert sich um die her, so ihn fürchten, und hilft ihnen aus.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Schmecket und sehet, wie freundlich der HERR ist! Wohl dem, der auf ihn trauet!
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Fürchtet den HERRN, ihr seine Heiligen; denn die ihn fürchten, haben keinen Mangel.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Die Reichen müssen darben und hungern; aber die den HERRN suchen, haben keinen Mangel an irgendeinem Gut.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Kommt her, Kinder, höret mir zu! Ich will euch die Furcht des HERRN lehren.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Wer ist, der gut Leben begehrt und gerne gute Tage hätte?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Behüte deine Zunge vor Bösem und deine Lippen, daß sie nicht falsch reden.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Laß vom Bösen und tue Gutes, suche Frieden und jage ihm nach.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Die Augen des HERRN sehen auf die Gerechten und seine Ohren auf ihr Schreien.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Das Antlitz aber des HERRN stehet über die, so Böses tun, daß er ihr Gedächtnis ausrotte von der Erde.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Wenn die (Gerechten) schreien, so höret der HERR und errettet sie aus all ihrer Not.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Der HERR ist nahe bei denen, die zerbrochenes Herzens sind, und hilft denen, die zerschlagen Gemüt haben.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Der Gerechte muß viel leiden; aber der HERR hilft ihm aus dem allem.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Er bewahret ihm alle seine Gebeine, daß deren nicht eins zerbrochen wird.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Den Gottlosen wird das Unglück töten, und die den Gerechten hassen, werden Schuld haben.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Psalm 34 >