< Psalm 147 >

1 Lobet den HERRN; denn unsern Gott loben, das ist ein köstlich Ding; solch Lob ist lieblich und schön.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 Der HERR bauet Jerusalem und bringet zusammen die Verjagten in Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Er heilet, die zerbrochenes Herzens sind, und verbindet ihre Schmerzen.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Er zählet die Sterne und nennet sie alle mit Namen.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Unser HERR ist groß und von großer Kraft; und ist unbegreiflich, wie er regieret.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 Der HERR richtet auf die Elenden und stößet die Gottlosen zu Boden.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Singet umeinander dem HERRN mit Dank und lobet unsern Gott mit Harfen,
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 der den Himmel mit Wolken bedeckt und gibt Regen auf Erden; der Gras auf Bergen wachsen läßt;
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 der dem Vieh sein Futter gibt, den jungen Raben, die ihn anrufen.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Er hat nicht Lust an der Stärke des Rosses noch Gefallen an jemandes Beinen.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Der HERR hat Gefallen an denen, die ihn fürchten, die auf seine Güte hoffen.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Preise, Jerusalem, den HERRN; lobe, Zion, deinen Gott!
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Denn er macht fest die Riegel deiner Tore und segnet deine Kinder drinnen.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 Er schaffet deinen Grenzen Frieden und sättiget dich mit dem besten Weizen.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Er sendet seine Rede auf Erden; sein Wort läuft schnell.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Er gibt Schnee wie Wolle, er streuet Reif wie Asche.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Er wirft seine Schloßen wie Bissen; wer kann bleiben vor seinem Frost?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Er spricht, so zerschmilzt es; er läßt seinen Wind wehen, so tauet's auf.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Er zeiget Jakob sein Wort, Israel seine Sitten und Rechte.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 So tut er keinen Heiden, noch läßt sie wissen seine Rechte. Halleluja!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalm 147 >