< Psalm 105 >

1 Danket dem HERRN und prediget seinen Namen; verkündiget sein Tun unter den Völkern;
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 singet von ihm und lobet ihn; redet von allen seinen Wundern;
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 rühmet seinen heiligen Namen; es freue sich das Herz derer, die den HERRN suchen!
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Fraget nach dem HERRN und nach seiner Macht; suchet sein Antlitz allewege!
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Gedenket seiner Wunderwerke, die er getan hat, seiner Wunder und seines Worts,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 ihr, der Same Abrahams, seines Knechts, ihr Kinder Jakobs, seine Auserwählten!
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Er ist der HERR, unser Gott; er richtet in aller Welt.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Er gedenket ewiglich an seinen Bund, des Worts, das er verheißen hat auf viel tausend für und für
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 den er gemacht hat mit Abraham, und des Eides mit Isaak,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 und stellete dasselbige Jakob zu einem Recht und Israel zum ewigen Bunde
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 und sprach: Dir will ich das Land Kanaan geben, das Los eures Erbes,
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 da sie wenig und geringe waren und Fremdlinge drinnen.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Und sie zogen von Volk zu Volk, von einem Königreiche zum andern Volk.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Er ließ keinen Menschen ihnen Schaden tun und strafte Könige um ihretwillen.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 Tastet meine Gesalbten nicht an und tut meinen Propheten kein Leid!
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Und er ließ eine Teurung ins Land kommen und entzog allen Vorrat des Brots.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Er sandte einen Mann vor ihnen hin; Joseph ward zum Knechte verkauft.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Sie zwangen seine Füße im Stock, sein Leib mußte in Eisen liegen,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 bis daß sein Wort kam und die Rede des HERRN ihn durchläuterte.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Da sandte der König hin und ließ ihn losgeben, der HERR über Völker hieß ihn auslassen.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Er setzte ihn zum HERRN über sein Haus, zum HERRSCher über alle seine Güter,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 daß er seine Fürsten unterweisete nach seiner Weise und seine Ältesten Weisheit lehrete.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Und Israel zog nach Ägypten, und Jakob ward ein Fremdling im Lande Hams.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Und er ließ sein Volk sehr wachsen und machte sie mächtiger denn ihre Feinde.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Er verkehrete jener Herz, daß sie seinem Volk gram wurden und dachten seine Knechte mit List zu dämpfen.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Er sandte seinen Knecht Mose, Aaron, den er hatte erwählet.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Dieselben taten seine Zeichen unter ihnen und seine Wunder im Lande Hams.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Er ließ Finsternis kommen und machte es finster; und waren nicht ungehorsam seinen Worten.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Er verwandelte ihre Wasser in Blut und tötete ihre Fische.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Ihr Land wimmelte Kröten heraus in den Kammern ihrer Könige.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Er sprach, da kam Ungeziefer, Läuse, in allen ihren Grenzen.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Er gab ihnen Hagel zum Regen, Feuerflammen in ihrem Lande;
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 und schlug ihre Weinstöcke und Feigenbäume und zerbrach die Bäume in ihren Grenzen.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Er sprach, da kamen Heuschrecken und Käfer ohne Zahl.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Und sie fraßen alles Gras in ihrem Lande und fraßen die Früchte auf ihrem Felde.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Und schlug alle Erstgeburt in Ägypten, alle ihre ersten Erben.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Und führete sie aus mit Silber und Golde; und war kein Gebrechlicher unter ihren Stämmen.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Ägypten ward froh, daß sie auszogen; denn ihre Furcht war auf sie gefallen.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Er breitete eine Wolke aus zur Decke und ein Feuer des Nachts zu leuchten.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Sie baten, da ließ er Wachteln kommen; und er sättigte sie mit Himmelbrot.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Er öffnete den Felsen, da flossen Wasser aus, daß Bäche liefen in der dürren Wüste.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Denn er gedachte an sein heiliges Wort, Abraham, seinem Knechte, geredet.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Also führete er sein Volk aus mit Freuden und seine Auserwählten mit Wonne
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 und gab ihnen die Länder der Heiden, daß sie die Güter der Völker einnahmen
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 auf daß sie halten sollten seine Rechte und seine Gesetze bewahren. Halleluja!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalm 105 >