< Psalm 104 >

1 Lobe den HERRN, meine Seele! HERR, mein Gott, du bist sehr herrlich; du bist schön und prächtig geschmückt.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Licht ist dein Kleid, das du anhast. Du breitest aus den Himmel wie einen Teppich;
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 du wölbest es oben mit Wasser; du fährest auf den Wolken wie auf einem Wagen und gehest auf den Fittichen des Windes
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 der du machest deine Engel zu Winden und deine Diener zu Feuerflammen;
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 der du das Erdreich gründest auf seinen Boden, daß es bleibt immer und ewiglich.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Mit der Tiefe deckest du es wie mit einem Kleid, und Wasser stehen über den Bergen.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Aber von deinem Schelten fliehen sie, von deinem Donner fahren sie dahin.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Die Berge gehen hoch hervor, und die Breiten setzen sich herunter zum Ort, den du ihnen gegründet hast.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Du hast eine Grenze gesetzt, darüber kommen sie nicht, und müssen nicht wiederum das Erdreich bedecken.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Du lässest Brunnen quellen in den Gründen, daß die Wasser zwischen den Bergen hinfließen,
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 daß alle Tiere auf dem Felde trinken und das Wild seinen Durst lösche.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 An denselben sitzen die Vögel des Himmels und singen unter den Zweigen.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Du feuchtest die Berge von oben her; du machest das Land voll Früchte, die du schaffest.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Du lässest Gras wachsen für das Vieh und Saat zu Nutz den Menschen, daß du Brot aus der Erde bringest,
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 und daß der Wein erfreue des Menschen Herz und seine Gestalt schön werde von Öl, und das Brot des Menschen Herz stärke;
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 daß die Bäume des HERRN voll Safts stehen, die Zedern Libanons, die er gepflanzet hat.
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 Daselbst nisten die Vögel, und die Reiher wohnen auf den Tannen.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 Die hohen Berge sind der Gemsen Zuflucht und die Steinklüfte der Kaninchen.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Du machest den Mond, das Jahr danach zu teilen; die Sonne weiß ihren Niedergang.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Du machest Finsternis, daß Nacht wird; da regen sich alle wilden Tiere,
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 die jungen Löwen, die da brüllen nach dem Raub und ihre Speise suchen von Gott.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Wenn aber die Sonne aufgehet, heben sie sich davon und legen sich in ihre Löcher.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 So gehet denn der Mensch aus an seine Arbeit und an sein Ackerwerk bis an den Abend.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 HERR, wie sind deine Werke so groß und viel! Du hast sie alle weislich geordnet und die Erde ist voll deiner Güter.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Das Meer, das so groß und weit ist, da wimmelt's ohne Zahl, beide große und kleine Tiere.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 Daselbst gehen die Schiffe; da sind Walfische, die du gemacht hast, daß sie drinnen scherzen.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Es wartet alles auf dich, daß du ihnen Speise gebest zu seiner Zeit.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Wenn du ihnen gibst, so sammeln sie; wenn du deine Hand auftust, so werden sie mit Gut gesättiget.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Verbirgest du dein Angesicht, so erschrecken sie; du nimmst weg ihren Odem, so vergehen sie und werden wieder zu Staub.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Du lässest aus deinen Odem, so werden sie geschaffen, und verneuerst die Gestalt der Erde.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Die Ehre des HERRN ist ewig; der HERR hat Wohlgefallen an seinen Werken.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 Er schauet die Erde an, so bebet sie; er rühret die Berge an, so rauchen sie.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Ich will dem HERRN singen mein Leben lang und meinen Gott loben, solange ich bin.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Meine Rede müsse ihm wohlgefallen. Ich freue mich des HERRN.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Der Sünder müsse ein Ende werden auf Erden, und die Gottlosen nicht mehr sein! Lobe den HERRN, meine Seele! Halleluja!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalm 104 >