< Sprueche 31 >

1 Dies sind die Worte des Königs Lamuel, die Lehre, die ihn seine Mutter lehrete:
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Ach, mein Auserwählter, ach, du Sohn meines Leibes, ach, mein gewünschter Sohn,
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 laß nicht den Weibern dein Vermögen und gehe die Wege nicht, darin sich die Könige verderben!
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 O, nicht den Königen, Lamuel, gib den Königen nicht Wein zu trinken noch den Fürsten stark Getränke.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Sie möchten trinken und der Rechte vergessen und verändern die Sache irgend der elenden Leute.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Gebet stark Getränke denen, die umkommen sollen, und den Wein den betrübten Seelen,
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 daß sie trinken und ihres Elendes vergessen und ihres Unglücks nicht mehr gedenken.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Tu deinen Mund auf für die Stummen und für die Sache aller, die verlassen sind.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Tu deinen Mund auf und richte recht und räche den Elenden und Armen.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Wem ein tugendsam Weib bescheret ist, die ist viel edler denn die köstlichsten Perlen.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Ihres Mannes Herz darf sich auf sie verlassen, und Nahrung wird ihm nicht mangeln.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Sie tut ihm Liebes und kein Leides sein Leben lang.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Sie gehet mit Wolle und Flachs um und arbeitet gerne mit ihren Händen.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Sie ist wie ein Kaufmannsschiff, das seine Nahrung von ferne bringt.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 Sie stehet des Nachts auf und gibt Futter ihrem Hause und Essen ihren Dirnen.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Sie denkt nach einem Acker und kauft ihn und pflanzt einen Weinberg von den Früchten ihrer Hände.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Sie gürtet ihre Lenden fest und stärkt ihre Arme.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Sie merkt, wie ihr Handel Frommen bringt; ihre Leuchte verlöscht des Nachts nicht.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Sie streckt ihre Hand nach dem Rocken, und ihre Finger fassen die Spindel.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Sie breitet ihre Hände aus zu dem Armen und reichet ihre Hand dem Dürftigen.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Sie fürchtet ihres Hauses nicht vor dem Schnee, denn ihr ganzes Haus hat zwiefache Kleider.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Sie macht ihr selbst Decken; weiße Seide und Purpur ist ihr Kleid.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Ihr Mann ist berühmt in den Toren, wenn er sitzt bei den Ältesten des Landes.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Sie macht einen Rock und verkauft ihn; einen Gürtel gibt sie dem Krämer.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Ihr Schmuck ist, daß sie reinlich und fleißig ist; und wird hernach lachen.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Sie tut ihren Mund auf mit Weisheit, und auf ihrer Zunge ist holdselige Lehre.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Sie schauet, wie es in ihrem Hause zugehet, und isset ihr Brot nicht mit Faulheit.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Ihre Söhne kommen auf und preisen sie selig; ihr Mann lobt sie.
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Viele Töchter bringen Reichtum; du aber übertriffst sie alle.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Lieblich und schön sein ist nichts; ein Weib, das den HERRN fürchtet, soll man loben.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Sie wird gerühmt werden von den Früchten ihrer Hände; und ihre Werke werden sie loben in den Toren.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Sprueche 31 >