< 4 Mose 33 >

1 Das sind die Reisen der Kinder Israel, die aus Ägyptenland gezogen sind nach ihrem Heer durch Mose und Aaron.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Und Mose beschrieb ihren Auszug, wie sie zogen, nach dem Befehl des HERRN, und sind nämlich dies die Reisen ihres Zugs.
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 Sie zogen aus von Raemses am fünfzehnten Tage des ersten Monden, des andern Tages der Ostern, durch eine hohe Hand, daß alle Ägypter sahen,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 und begruben eben die Erstgeburt, die der HERR unter ihnen geschlagen hatte; denn der HERR hatte auch an ihren Göttern Gerichte geübt.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Als sie von Raemses auszogen, lagerten sie sich in Suchoth.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Und zogen aus von Suchoth und lagerten in Etham, welches liegt an dem Ende der Wüste.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Von Etham zogen sie aus und blieben im Grunde Hiroth, welches liegt gegen Baal-Zephon, und lagerten sich gegen Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Von Hiroth zogen sie aus und gingen mitten durchs Meer in die Wüste; und reiseten drei Tagereisen in der Wüste Etham und lagerten sich in Mara.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Von Mara zogen sie aus und kamen gen Elim, darin waren zwölf Wasserbrunnen und siebenzig Palmen; und lagerten sich daselbst.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Von Elim zogen sie aus und lagerten sich an das Schilfmeer.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Von dem Schilfmeer zogen sie aus und lagerten sich in der Wüste Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Von der Wüste Sin zogen sie aus und lagerten sich in Daphka.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 Von Daphka zogen sie aus und lagerten sich in Alus.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 Von Alus zogen sie aus und lagerten sich in Raphidim; daselbst hatte das Volk kein Wasser zu trinken.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Von Raphidim zogen sie aus und lagerten sich in der Wüste Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Von Sinai zogen sie aus und lagerten sich in die Lustgräber.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Von den Lustgräbern zogen sie aus und lagerten sich in Hazeroth.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Von Hazeroth zogen sie aus und lagerten sich in Rithma.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 Von Rithma zogen sie aus und lagerten sich in Rimon-Parez.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Von Rimon-Parez zogen sie aus und lagerten sich in Libna.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Von Libna zogen sie aus und lagerten sich in Rissa.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 Von Rissa zogen sie aus und lagerten sich in Kehelatha.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Von Kehelatha zogen sie aus und lagerten sich im Gebirge Sapher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Vom Gebirge Sapher zogen sie aus und lagerten sich in Harada.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Von Harada zogen sie aus und lagerten sich in Makeheloth.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 Von Makeheloth zogen sie aus und lagerten sich in Thahath.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Von Thahath zogen sie aus und lagerten sich in Tharah.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Von Tharah zogen sie aus und lagerten sich in Mithka.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 Von Mithka zogen sie aus und lagerten sich in Hasmona.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Von Hasmona zogen sie aus und lagerten sich in Moseroth.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Von Moseroth zogen sie aus und lagerten sich in Bne-Jakan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Von Bne-Jakan zogen sie aus und lagerten sich in Horgidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 Von Horgidgad zogen sie aus und lagerten sich in Jathbatha.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Von Jathbatha zogen sie aus und lagerten sich in Abrona.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Von Abrona zogen sie aus und lagerten sich in Ezeon-Gaber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 Von Ezeon-Gaber zogen sie aus und lagerten sich in der Wüste Zin, das ist Kades.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 Von Kades zogen sie aus und lagerten sich an dem Berge Hor, an der Grenze des Landes Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Da ging der Priester Aaron auf den Berg Hor nach dem Befehl des HERRN und starb daselbst im vierzigsten Jahr des Auszugs der Kinder Israel aus Ägyptenland, am ersten Tage des fünften Monden,
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 da er hundert und dreiundzwanzig Jahre alt war.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Und Arad der König der Kanaaniter, der da wohnete gegen Mittag des Landes Kanaan, hörete, daß die Kinder Israel kamen.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Und von dem Berge Horzogen sie aus und lagerten sich in Zalmona.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Von Zalmona zogen sie aus und lagerten sich in Phunon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Von Phunon zogen sie aus und lagerten sich in Oboth.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 Von Oboth zogen sie aus und lagerten sich in Jgim, am Gebirge Abarim in der Moabiter Grenze.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Von Jgim zogen sie aus und lagerten sich in Dibon-Gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 Von Dibon-Gad zogen sie aus und lagerten sich in Almon-Diblathaim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Von Almon-Diblathaim zogen sie aus und lagerten sich in dem Gebirge Abarim gegen Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 Von dem Gebirge Abarim zogen sie aus und lagerten sich in das Gefilde der Moabiter an dem Jordan gegen Jericho.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Sie lagerten sich aber am Jordan von Beth-Jesimoth bis an die Breite Sittim, des Gefildes der Moabiter.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 Und der HERR redete mit Mose in dem Gefilde der Moabiter an dem Jordan gegen Jericho und sprach:
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Rede mit den Kindern Israel und sprich zu ihnen: Wenn ihr über den Jordan gegangen seid in das Land Kanaan
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 so sollt ihr alle Einwohner vertreiben vor eurem Angesicht und alle ihre Säulen und alle ihre gegossenen Bilder umbringen und alle ihre Höhen vertilgen,
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 daß ihr also das Land einnehmet und drinnen wohnet; denn euch habe ich das Land gegeben, daß ihr's einnehmet.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Und sollt das Land austeilen durchs Los unter eure Geschlechter. Denen, deren viel ist, sollt ihr desto mehr zuteilen, und denen, deren wenig ist, sollt ihr desto weniger zuteilen. Wie das Los einem jeglichen daselbst fällt, so soll er's haben, nach den Stämmen ihrer Väter.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 Werdet ihr aber die Einwohner des Landes nicht vertreiben vor eurem Angesicht, so werden euch die, so ihr überbleiben lasset, zu Dornen werden in euren Augen und zu Stacheln in euren Seiten und werden euch drängen auf dem Lande, da ihr innen wohnet.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 So wird's denn gehen, daß ich euch gleich tun werde, was ich gedachte ihnen zu tun.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”

< 4 Mose 33 >