< 1 Mose 10 >

1 Dies ist das Geschlecht der Kinder Noahs: Sem, Ham, Japheth. Und sie zeugeten Kinder nach der Sintflut.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 Die Kinder Japheths sind diese: Gomer, Magog, Madai, Javan, Thubal, Mesech und Thiras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 Aber die Kinder von Gomer sind diese: Askenas, Riphath und Thogarma.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 Die Kinder von Javan sind diese: Elisa, Tharsis, Kittim und Dodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 Von diesen sind ausgebreitet die Inseln der Heiden in ihren Ländern, jegliche nach ihrer Sprache, Geschlecht und Leuten.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 Die Kinder von Ham sind diese: Chus, Mizraim, Put und Kanaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 Aber die Kinder von Chus sind diese. Seba, Hevila, Sabtha, Raema und Sabtecha. Aber die Kinder von Raema sind diese: Scheba und Dedan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 Chus aber zeugete den Nimrod. Der fing an ein gewaltiger HERR zu sein auf Erden,
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 und war ein gewaltiger Jäger vor dem HERRN. Daher spricht man: Das ist ein gewaltiger Jäger vor dem HERRN, wie Nimrod.
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 Und der Anfang seines Reichs war Babel, Erech, Ackad und Kalne im Lande Sinear.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 Von dem Land ist danach kommen der Assur und bauete Ninive und Rehoboth-Ir und Kalah,
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 dazu Resen zwischen Ninive und Kalah. Dies ist eine große Stadt.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 Mizraim zeugete Ludim, Anamim, Leabim, Naphthuhim,
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 Pathrusim und Kasluhim. Von dannen sind kommen die Philistim und Kaphthorim.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 Kanaan aber zeugete Zidon, seinen ersten Sohn, und Heth,
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 Jebusi, Emori, Girgasi,
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 Hivi, Arki, Sini,
Ahivi, Aariki, Asini,
18 Arvadi, Zemari und Hamathi. Daher sind ausgebreitet die Geschlechter der Kanaaniter.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 Und ihre Grenzen waren von Zidon an durch Gerar bis gen Gasa, bis man kommt gen Sodoma, Gomorrha, Adama, Zeboim und bis gen Lasa.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 Das sind die Kinder Hams in ihren Geschlechtern, Sprachen, Ländern und Leuten.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 Sem aber, Japheths, des größern, Bruder, zeugete auch Kinder, der ein Vater ist aller Kinder von Eber.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 Und dies sind seine Kinder: Elam, Assur, Arphachsad, Lud und Aram.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 Die Kinder aber von Aram sind diese: Uz, Hut, Gether und Mas.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 Arphachsad aber zeugete Salah, Salah zeugete Eber.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 Eber zeugete zween Söhne. Einer hieß Peleg, darum daß zu seiner Zeit die Welt zerteilet ward; des Bruder hieß Jaketan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 Und Jaketan zeugete Almodad, Saleph, Hazarmaveth, Jarah,
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 Hadoram, Usal, Dikela,
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 Obal, Abimael, Seba,
Obali, Abimaeli, Seba,
29 Ophir, Hevila und Jobab. Das sind alle Kinder von Jaketan.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 Und ihre Wohnung war von Mesa an, bis man kommt gen Sephar, an den Berg gegen den Morgen.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 Das sind die Kinder von Sem in ihren Geschlechtern, Sprachen, Ländern und Leuten.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 Das sind nun die Nachkommen der Kinder Noahs in ihren Geschlechtern und Leuten. Von denen sind ausgebreitet die Leute auf Erden nach der Sintflut.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< 1 Mose 10 >