< 1 Chronik 24 >

1 Aber dies war die Ordnung der Kinder Aaron. Die Kinder Aarons waren: Nadab, Abihu, Eleasar und Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Aber Nadab und Abihu starben vor ihrem Vater und hatten keine Kinder. Und Eleasar und Ithamar wurden Priester.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Und David ordnete sie also: Zadok aus den Kindern Eleasars und Ahimelech aus den Kindern Ithamars nach ihrer Zahl und Amt.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Und wurden der Kinder Eleasars mehr funden zu vornehmsten starken Männern denn der Kinder Ithamars. Und er ordnete sie also: nämlich sechzehn aus den Kindern Eleasars zu Obersten unter ihrer Väter Haus und acht aus den Kindern Ithamars unter ihrer Väter Haus.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Er ordnete sie aber durchs Los darum, daß beide aus Eleasars und Ithamars Kindern Oberste waren im Heiligtum und Oberste vor Gott.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Und der Schreiber Semaja, der Sohn Nethaneels, aus den Leviten, beschrieb sie vor dem Könige und vor den Obersten und vor Zadok, dem Priester, und vor Ahimelech, dem Sohne Abjathars, und vor den obersten Vätern unter den Priestern und Leviten; nämlich ein Vaterhaus für Eleasar und das andere für Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Und das erste Los fiel auf Jojarib, das andere auf Jedaja,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 das dritte auf Harim, das vierte auf Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 das fünfte auf Malchija, das sechste auf Mejamin,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 das siebente auf Hakoz, das achte auf Abia,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 das neunte auf Jesua, das zehnte auf Sechanja,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 das elfte auf Eliasib, das zwölfte auf Jakim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 das dreizehnte auf Hupa, das vierzehnte auf Jesebeab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 das fünfzehnte auf Bilga, das sechzehnte auf Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 das siebenzehnte auf Hesir, das achtzehnte auf Hapizez,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 das neunzehnte auf Pethahja, das zwanzigste auf Jeheskel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 das einundzwanzigste auf Jachin, das zweiundzwanzigste auf Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 das dreiundzwanzigste auf Delaja, das vierundzwanzigste auf Maasia.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Das ist ihre Ordnung nach ihrem Amt, zu gehen in das Haus des HERRN, nach ihrer Weise unter ihrem Vater Aaron, wie ihnen der HERR, der Gott Israels, geboten hat.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Aber unter den andern Kindern Levi war unter den Kindern Amrams Subael. Unter den Kindern Subaels war Jehdea.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Unter den Kindern Rehabjas war der erste Jesia.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Aber unter den Jezeharitern war Slomoth. Unter den Kindern Slomoths war Jahath.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 Die Kinder Hebrons waren: Jeria der erste, Amarja der andere, Jahesiel der dritte, Jakmeam der vierte.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Die Kinder Usiels waren Micha. Unter den Kindern Michas war Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Der Bruder Michas war Jesia. Unter den Kindern Jesia war Sacharja.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Die Kinder Meraris waren: Maheli und Musi, des Sohn war Jaesia.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Die Kinder Meraris von Jaesia, seinem Sohn, waren: Soham, Sakur und Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Maheli aber hatte Eleasar; denn er hatte keine Söhne.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Von Kis. Die Kinder Kis waren: Jerahmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Die Kinder Musis waren: Maheli, Eder und Jerimoth. Das sind die Kinder der Leviten unter ihrer Väter Haus.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Und man warf für sie auch das Los neben ihren Brüdern, den Kindern Aaron, vor dem Könige David und Zadok und Ahimelech und vor den obersten Vätern unter den Priestern und Leviten, dem kleinsten Bruder ebensowohl als dem Obersten unter den Vätern.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronik 24 >