< Psalm 85 >
1 Dem Musikmeister. Von den Korachiten. Ein Psalm. Du hast dein Land begnadigt, Jahwe, hast das Geschick Jakobs gewendet.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Du hast die Verschuldung deines Volks hinweggenommen, hast alle ihre Sünde vergeben. (Sela)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Du hast allen deinen Grimm zurückgezogen, hast abgelassen von der Glut deines Zorns.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Stelle uns wieder her, Gott, der du unsere Hilfe bist, und laß deinen Unmut gegen uns fahren.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Willst du denn ewig über uns zürnen, deinen Zorn auf alle künftigen Geschlechter ausdehnen?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Willst du uns nicht wieder aufleben lassen, daß sich dein Volk über dich freuen möge?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Jahwe, laß uns deine Gnade schauen und schenke uns dein Heil!
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Ich will doch hören, was Gott Jahwe redet; er redet von Frieden zu seinem Volk und zu seinen Frommen und zu denen, die ihr Herz ihm zuwenden.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Ja, seine Hilfe ist nahe denen, die ihn fürchten, daß Herrlichkeit in unserem Lande wohne.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Gnade und Treue begegnen einander, Gerechtigkeit und Friede küssen sich.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Treue sproßt aus der Erde hervor, und Gerechtigkeit schaut vom Himmel herab.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Ja, Jahwe wird Gutes gewähren, und unser Land wird sein Gewächs geben.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Gerechtigkeit geht vor ihm her und achtet auf die Richtung seiner Tritte.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.