< Psalm 145 >
1 Ein Lobgesang Davids. Ich will dich erheben, mein Gott, du König, und deinen Namen immer und ewig preisen!
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Tag für Tag will ich dich preisen und deinen Namen immer und ewig rühmen.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Jahwe ist groß und hoch zu rühmen, und seine Größe ist unausforschlich.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Ein Geschlecht rühme dem anderen deine Werke und verkündige deine gewaltigen Thaten.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Von der Hoheit deiner majestätischen Herrlichkeit sollen sie reden; von deinen Wundern will ich sprechen.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Von der Gewalt deiner furchtbaren Thaten sollen sie sagen, und deine großen Thaten, die will ich erzählen.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Das Gedächtnis deiner großen Güte sollen sie ausströmen und über deine Gerechtigkeit jubeln.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Gnädig und barmherzig ist Jahwe, langsam zum Zorn und von großer Gnade.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Jahwe ist allen gütig, und sein Erbarmen erstreckt sich über alle seine Werke.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Es sollen dich loben, Jahwe, alle deine Werke, und deine Frommen dich preisen.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Von der Herrlichkeit deines Königtums sollen sie sagen und von deiner Gewalt reden,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 daß sie den Menschenkindern seine gewaltigen Thaten kund thun und die majestätische Hoheit seines Königtums.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Dein Reich ist ein Reich für alle Ewigkeit, und deine Herrschaft währt durch alle Geschlechter. Wahrhaftig ist Jahwe in allen seinen Worten und gnädig in allen seinen Thaten.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Jahwe stützt alle, die da fallen, und richtet alle Gebeugten auf.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Aller Augen warten auf dich, und du giebst ihnen ihre Speise zu seiner Zeit.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Du thust deine Hand auf und sättigst alles Lebendige mit Wohlgefallen.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Jahwe ist gerecht in allen seinen Wegen und gnädig in allen seinen Thaten.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Jahwe ist nahe allen, die ihn anrufen, allen, die ihn mit Ernst anrufen.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Er thut nach dem Willen derer, die ihn fürchten, und hört ihr Geschrei und hilft ihnen.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Jahwe behütet alle, die ihn lieben, aber alle Gottlosen vertilgt er.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Mein Mund soll vom Ruhm Jahwes reden, und alles Fleisch preise seinen heiligen Namen immer und ewig!
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.