< Psalm 121 >

1 Ein Lied für die Wallfahrten. Ich hebe meine Augen zu den Bergen auf: von wo wird Hilfe für mich kommen?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Meine Hilfe kommt von Jahwe, dem Schöpfer Himmels und der Erde.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Er wird deinen Fuß nimmermehr wanken lassen; dein Hüter schläft nicht.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Fürwahr, nicht schläft, noch schlummert der Hüter Israels.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Jahwe ist dein Hüter, Jahwe dein Schatten zu deiner rechten Hand.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Am Tage wird dich die Sonne nicht stechen, noch der Mond des Nachts.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Jahwe wird dich behüten vor allem Übel, wird deine Seele behüten.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Jahwe wird dein Aus- und Eingehen behüten von nun an bis in Ewigkeit.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Psalm 121 >