< Psalm 67 >
1 Auf den Siegesspender, mit Zithern, ein Lied, ein Gesang. Gott sei uns gnädig, segne uns! Er lasse uns sein Antlitz leuchten. (Sela)
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 Wenn man auf Erden Deine Weise kennenlernt, bei all den Heiden Deine hilfereiche Art,
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 dann preisen Dich die Völker, Gott, dann preisen Dich die Völker all.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Dann freuen sich und jubeln die Nationen, daß Du gerecht die Völker richtest, auf Erden die Nationen leitest. (Sela)
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Dann preisen Dich die Völker, Gott; dann preisen Dich die Völker all.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Die Erde spendet ihre Ernte! Uns segnet Gott ja, unser Gott!
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 Uns segne fürder Gott, daß sich die Erdenenden alle vor ihm fürchten!
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.