< Psalm 54 >

1 Auf den Siegesspender, bei Saitenspiel, ein Lehrgedicht, von David, als die Ziphiter zu Saul kamen und sagten "HäIt bei uns sich David nicht verborgen?" Hilf mir, o Gott, durch Deinen Namen! Verschaff mir Recht durch Deine Stärke!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Gott! Höre mein Gebet! Vernimm die Worte meines Mundes'
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Erheben Fremdlinge sich gegen mich und trachten Mächtige mir nach dem Leben und stellen Gott sich nicht vor Augen, (Sela)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 so ist mir Gott ein Helfer. Der Herr bleibt der Beschirmer meines Lebens.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Auf meine Feinde falle Ungemach zurück! Vertilge sie nach Deiner Treue!
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Ein reichlich Opfer bringe ich Dir darund rühme Deinen Namen, Herr, daß er so gütig ist.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 Er rettet mich aus aller Not; mein Auge weidet sich an meinen Feinden.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Psalm 54 >