< Psalm 34 >

1 Von David, als er seinen Verstand vor Abimelech verstellte und dieser ihn verjagte, worauf er sich entfernte. Lobpreisen will ich jederzeit den Herrn. Sein Lob sei stets in meinem Munde!
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Es rühme meine Seele sich im Herrn! Die Armen sollen's hören und sich freuen!
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Verherrlichet den Herrn mit mir! Laßt uns gemeinsam seinen Namen preisen!
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Den Herrn such ich auf; er hört auf mich, befreit mich aus den Ängsten all.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Mich schauet an und strahlt vor Freude! Nie röte mehr sich euer Angesicht!
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Hier ist ein armer Mensch, der einst gerufen. Der Herr vernahm's und half ihm aus den Nöten all.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Des Herrn Engel lagert sich um jene, die ihn fürchten, er rettet sie.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 So kostet und erfahrt, wie gut der Herr! Wie wohl dem Mann, der ihm vertraut!
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Vorm Herrn habt Furcht, ihr, seine Heiligen! Denn die ihn fürchten, leiden keinen Mangel.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Die Gottesleugner hungern darbend; doch denen, die den Herrn aufsuchen, mangelt nicht, was ihnen frommt.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Her, Kinder, hört mir zu! Ich lehre euch die Furcht des Herrn.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Wer ist der Mann, der Lust zum Leben hat, der zum Genuß des Glückes leben möchte?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Behüte vor dem Bösen deine Zunge, vor trügerischer Rede deine Lippen!
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Vom Bösen laß und tu das Gute! den Frieden such! Ihm jage nach!
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Des Herrn Augen achten auf die Frommen und seine Ohren auf ihr Flehen.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Des Herrn Antlitz wendet sich den Übeltätern zu und tilgt ihr Angedenken von der Erde.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Die Frommen schreien, und schon hört's der Herr und rettet sie aus aller Not.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Der Herr ist nahe den zerknirschten Herzen; zerschlagenen Gemütern hilft er auf.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 In viel Gefahren ist der Fromme; aus ihnen allen rettet ihn der Herr.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Er hütet jedes seiner Glieder; versehrt wird auch nicht eins davon.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Den Frevler rafft ein Unfall weg; des Frommen Hasser müssen es bereuen.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Der Herr erlöst die Seele seiner Diener; wer auf ihn baut, bereut es nicht.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

< Psalm 34 >