< Psalm 20 >
1 Auf den Siegesspender, ein Lied, von David. Der Herr erhöre dich noch an dem Tag der Not! Des Gottes Jakobs Name schütze dich!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Er sende aus dem Heiligtum dir Hilfe und stütze dich von Sion her!
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Er nehme an all deine Opfergaben und freue sich an deinen Brandopfern! (Sela)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Er gebe dir, was nur dein Herz begehrt; und lasse alle deine Pläne wohl gelingen!
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Dann jauchzen wir ob deines Sieges und jubeln laut in unseres Gottes Namen. Der Herr erfülle dir die Wünsche all! -
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 jetzt weiß ich es: Der Herr hilft dem, den er gesalbt, erhört ihn von dem heiligen Himmel her mit hilfereichen Taten seiner Rechten.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Sind jene noch so stolz auf Wagen und auf Rosse, wir sind es auf den Namen unsres Herrn und Gottes.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Sie krümmen sich und stürzen hin; wir aber stehen wieder auf.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Herr, hilf dem Königund höre uns, sooft wir rufen!
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!