< Psalm 109 >

1 Auf den Siegesspender, von David, ein Lied. - Mein Gott, den ich lobpreise, sei nicht taub!
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Sie öffnen gegen mich den frechen, falschen Mund; mit Lügenzungen reden sie zu nur
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 und überhäufen mich mit Hassesworten und feinden ohne Grund mich an.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 Für meine Liebe klagen sie mich an; ich muß mich gar verteidigen.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Für Gutes haben sie für mich nur böse Wünsche, für meine Liebe Haß: -
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 "Man möge einen Frevler gegen ihn bestellen, daß er als Kläger gegen ihn auftrete!
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Er gehe schuldig im Gericht hervor; fehlschlage ihm sein Rechten!
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Nur wenig seien seine Tage; ein anderer nehme sein Erspartes!
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Und seine Kinder sollen Waisen werden und seine Gattin Witwe!
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Unstet umherziehen und betteln sollen seine Kinder, aus ihren leeren Wohnungen verstoßen werden!
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Ein Wucherer belege seine ganze Habe mit Beschlag, und Fremde sollen sein Erworbnes plündern!
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Nicht einer bleibe ihm gewogen! Nicht einer schenke Mitleid seinen Waisen!
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Sein Stamm verfalle der Vernichtung; im zweiten Glied erlösche schon sein Name!
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Beim Herrn werd seiner Väter Schuld gedacht, und seiner Mutter Sünde werde nimmer ausgelöscht!
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Sie seien stets dem Herrn vor Augen, daß er vertilge ihr Gedächtnis von der Erde.
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Denn er gedachte nimmer, Liebe zu erweisen, verfolgte elende und arme Leute und gab den Todesstoß zerbrochenen Herzen.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Weil ihm der Fluch so lieb und ihm sich leicht einstellte, dieweil das Segnen er nicht mochte, weil's ihm ferne lag,
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 dieweil den Fluch er wie sein eigen Kleid anlegte, wie Wasser in sein Inneres nahm und er wie Öl in seine Glieder drang,
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 so sei er ihm wie ein Gewand, das er als Hülle um sich legt, gleich einem Gürtel, den er ständig trägt!" -
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Vom Herrn geschehe also meinen Anklägern, die wider mich gar Schlimmes reden!
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Du aber, Herr, mein Gott, befasse Dich mit mir um Deines Namens willen! Errette mich nach Deiner milden Huld!
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Denn ich bin bettelarm und leidend; mein Herz bricht mir im Leibe.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Gleich einem Schatten, der sich neigt, vergehe ich, bin hohl gleich einem Rauchfang.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Vor Fasten wanken mir die Knie; mein Leib zehrt ab, wird mager.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Ich bin ihr Spott; sie sehen mich und schütteln ihren Kopf. -
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Komm mir zu Hilfe, Herr, mein Gott! Errette mich nach Deiner Huld,
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 damit sie innewerden, Deine Hand sei es, daß Du, Herr, solches tust!
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Sie mögen fluchen! Doch Du segne! So werden meine Widersacher voller Scham, Dein Diener aber voller Freude.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 In Schande müssen meine Ankläger sich kleiden, in ihre Scham sich hüllen wie in einen Mantel! -
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Dann danke ich dem Herrn mit lautem Munde und preise ihn inmitten Vieler,
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 daß er dem Armen steht zur Rechten, zur Hilfe gegen die, die ihn verklagen.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Psalm 109 >