< Sprueche 3 >

1 Mein Sohn, vergiß nicht meine Weisung! Dein Herz beachte mein Gebot!
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Denn viele Tage, lange Lebensjahre verheißen sie in Fülle dir und Wohlfahrt.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Sie mögen dich in treuer Liebe nicht verlassen! Bind um den Hals sie, schreibe sie auf deines Herzens Tafeln!
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Durch feine Lebensart gewinnst du Gunst in Gottes und der Menschen Augen.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Auf Gott vertrau von ganzem Herzen! Stütz dich auf eigene Einsicht nie!
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Auf allen deinen Wegen denk an ihn! Dann ebnet er dir deine Pfade.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Halt dich nicht selbst für weise! Fürchte den Herrn! Halt ferne dich vom Bösen!
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Erquickung sei dies deinem Leibe und Labsal deinen Gliedern!
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Ehre den Herrn mit deiner Habe, mit deiner ganzen Ernte erstem Abhub!
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Dann werden reichlich deine Scheunen voll; vom Moste strömen deine Kufen.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Die Zucht des Herrn verachte nicht, mein Sohn, und seufze niemals über seine Strafe!
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Denn wen der Herr liebhat, den züchtigt er, so wie ein Vater seinen Sohn, an dem er Wohlgefallen hat.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Heil sei dem Mann, der Weisheit findet, dem Mann, der Einsicht sich erwirbt!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Denn was sie einbringt, übertrifft, was man am Silber haben kann, und was sie abwirft, übertrifft, was man um Gold erwirbt.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Sie ist weit köstlicher als Perlen, und gar nichts kommt ihr gleich, was du dir wünschen könntest.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 In ihrer rechten Hand liegt langes Leben, in ihrer linken Reichtum und Besitz.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 All ihre Wege sind der Wohlfahrt Wege; all ihre Pfade sind nur Heil.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Ein Lebensbaum für den, der sie ergreift, und wer sie festhält, ist beglückt.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Durch Weisheit gründete der Herr die Erde; durch Einsicht machte er den Himmel fest.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Durch seine Kunst ergießen sich die Ozeane und senden Wolken Tau herab.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mein Sohn! Laß sie nicht aus den Augen! Bewahre Umsicht, klugen Rat!
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 So werden sie für dich zum Leben, für deinen Hals zu anmutsvollem Schmuck.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Dann gehst du sicher deines Weges; dein Fuß stößt nirgends an.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Wenn du dich niederlegst, dann brauchst du keine Furcht zu haben, und wenn du schläfst, ist süß dein Schlummer.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Vor plötzlichem Erschrecken brauchst du dich nicht zu ängstigen, nicht vor dem Unheil für den Frevler, daß es käme.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Der Herr ist deine Zuversicht: Er hütet vor Verstrickung deinen Fuß.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Versag nicht dem die Wohltaten, der sie verdient, wenn es in deiner Macht steht, sie zu spenden!
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Sag nicht zu deinem Nächsten: "Geh fort! Komm später! Ich geb dir morgen etwas", wenn du es heute kannst.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ersinn nicht Böses gegen deinen Nächsten, vor allem nicht, solang er arglos bei dir wohnt!
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Mit keinem Menschen streite ohne Grund, wenn er dir nichts zuleid getan!
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Beneide nicht die Herrenmenschen, wähl keinen ihrer Wege!
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Der Arge ist dem Herrn ein Greuel; ein Freund ist er den aufrichtigen Seelen.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Der Fluch des Herrn ruht auf des Frevlers Haus; der Frommen Wohnstatt segnet er.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Der Mühe, die sich Spötter machen, spottet er; den frommen Duldern gibt er reichlich.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Den Weisen kommt die Ehre zu; die Toren kommen an den Pranger.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Sprueche 3 >