< Nehemia 7 >
1 Als die Mauer erbaut war, setzte ich die Tore ein. Dann wurden die Torhüter, die Leviten, für ihr Amt ernannt.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Meinen Bruder Chanani, auch Chananja genannt, bestellte ich zum Burgherrn über Jerusalem. Er galt bei vielen als ein zuverlässiger und gottesfürchtiger Mann.
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 Ich sprach zu ihnen: "Man öffne nicht die Tore Jerusalems, bis die Sonne scheint, und bis sie aufgestanden sind, halte man die Tore verschlossen Haltet fest daran! Für die Bewohner Jerusalems stelle man Wachen auf, je einen auf seinen Posten und je einen vor dem Hause."
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Nun war die Stadt ausgedehnt und groß. Aber nur wenige Leute waren darin. Noch waren keine Häuser gebaut.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Da gab mein Gott mir ins Herz, die Adligen und Vorsteher und das Volk zu versammeln und sie nach ihrer Abkunft aufzuzeichnen. Dabei fand ich das Geschlechterverzeichnis derer, die zuerst heraufgezogen waren. Ich fand geschrieben:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Dies sind die Söhne der Landschaft, die aus der Gefangenschaft der Exulanten hergezogen sind, die einstens Babels König Nebukadrezar weggeführt hat, und die nach Jerusalem und Juda zurückkehrten, jeder in seine Stadt,
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 die mit Zerubbabel, Jesua, Nechemja, Azarja, Reamja, Nachamani, Mordekai, Bilsan, Misperet, Bigwai, Nechum und Baana gekommen sind, die Zahl der Männer des Volkes Israel:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 die Söhne des Paros 2.172,
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 die Söhne Sephatjas 372,
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 die Söhne des Arach 652,
Zidzukulu za Ara 652
11 die Söhne des Pachatmoab (Moabs Statthalter), nämlich die Söhne des Jesua und Joab 2.818,
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 die Söhne des Elam 1.254,
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 die Söhne des Zattu 845,
Zidzukulu za Zatu 845
14 die Söhne des Zakkai 760,
Zidzukulu za Zakai 760
15 die Söhne des Binnui 648,
Zidzukulu za Binuyi 648
16 die Söhne des Bebai 628,
Zidzukulu za Bebai 628
17 die Söhne des Azgad 2.322,
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 die Söhne des Adonikam 667,
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 die Söhne des Bigwai 2.067,
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 die Söhne des Adin 655,
Zidzukulu za Adini 655
21 die Söhne des Ater von Chizkija 98,
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 die Söhne des Chasum 328,
Zidzukulu za Hasumu 328
23 die Söhne des Besai 324,
Zidzukulu za Bezayi 324
24 die Söhne des Chariph 112,
Zidzukulu za Harifu 112
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 die Männer von Bethlehem und Netopha 188,
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 die Männer von Anatot 128,
Anthu a ku Anatoti 128
28 die Männer von Bet-Azmawet 42,
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 die Männer von Kirjatjearim, Kephira und Beerot 743,
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 die Männer der Rama und von Geba 621,
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 die Männer von Mikmas 122,
Anthu a ku Mikimasi 122
32 die Männer von Betel und dem Ai 123,
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 die Männer von Neu Nebo 52,
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 die Söhne Neu Elams 1.254,
Ana a Elamu wina 1,254
35 die Söhne Charims 320,
Zidzukulu za Harimu 320
36 die Söhne Jerichos 345,
Zidzukulu za Yeriko 345
37 die Söhne des Lod, Chadid und Ono 721,
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 die Söhne Senaas 3930,
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 die Priester: die Söhne Jedajas vom Hause Jesua 973,
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 die Söhne des Immer 1.052,
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 die Söhne des Paschur 1.247,
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 die Söhne des Charim 1.017,
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 die Leviten: die Söhne des Jesua, nämlich Kadmiel, die Söhne Hodewas 74,
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 die Sänger: die Söhne Asaphs 148,
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 die Torhüter: die Söhne Sallums, die Söhne Aters, die Söhne Talmons, die Söhne Akkubs, die Söhne Chatitas, die Söhne Sobais 138,
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 die Tempelsklaven: die Söhne des Sicha, die Söhne des Chasupha, die des Tabbaot,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 die Söhne des Keros, die des Sia, die des Paddon,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 die Söhne des Lebana, die des Chazaba, die des Salmai,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 die Söhne des Chanan, die des Giddel, die des Gachar,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 die Söhne des Reaja, die des Resin, die des Nekoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 die Söhne des Gazzam, die des Uzza, die des Peseach,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 die Söhne des Besai, die der Mëuniter, die der Nephisiter,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 die Söhne des Bakbuk, die des Chakupha, die des Charchur,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 die Söhne des Baslit, die des Mechida, die des Charsa,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 die Söhne des Barkos, die des Sisera, die des Temach,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 die Söhne des Nesiach, die des Chatipha,
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 die Söhne der Sklaven Salomos: die Söhne des Sotai, die Sopherets (der Schreiberin), die des Perida,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 die Söhne des Jaala, die des Darkon, die des Giddel,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 die Söhne des Sephatja, die des Chattil, die Söhne der Pokeret der Gazellen, die des Amon,
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 alle Tempelsklaven und Söhne der Sklaven Salomos 392.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Dies sind die, die aus Tel Melach, Tel Charsa, Cherub, Addon und Immer hergezogen sind, aber nicht haben dartun können, ob ihr Haus und ihre Abstammung israelitisch seien:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 die Söhne des Delaja, die des Tobia und die des Nekoda 642,
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 und von den Priestern die Söhne des Chabaja, die des Hakkos und die Söhne Barzillais, der eine von den Töchtern des Gileaditers Barzillai sich zum Weibe genommen hatte und dann nach ihrem Namen benannt ward.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Diese hatten ihre Geschlechtsurkunde gesucht. Sie fand sich aber nicht vor, und so wurden sie vom Priestertum ausgeschlossen.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Da sprach der Tirsata zu ihnen, sie dürften vom Hochheiligen so lange nicht essen, bis daß ein Priester für Urim und Tummim erstünde.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Die ganze Gemeinde, alles in allem, belief sich auf 42.360,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 nicht eingerechnet ihre Sklaven und die Sklavinnen, an Zahl 7.387; auch hatten sie 200 Sänger und Sängerinnen.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Und ihrer Pferde waren es 736, ihrer Maultiere 245,
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 ihrer Kamele 435, ihrer Esel 6.720.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Und einige von den Familienhäuptern spendeten in den Werkschatz; der Tirsata spendete für den Schatz an Gold 1.000 Drachmen, 50 Sprengschalen, 530 Priesterkleider.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 Einige von den Familienhäuptern spendeten in den Werkschatz an Gold 20.000 Drachmen und an Silber 2.200 Minen.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Und was das übrige Volk gab, betrug an Gold 20.000 Drachmen und an Silber 2.000 Minen und was das übrige Volk gab, betrug an Gold 20.000 Drachmen, an Silber 2.000 und 67 Priesterkleider.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Die Priester aber und die Leviten, die Torhüter, die Sänger und die Leute aus dem Volke sowie die Tempelsklaven und ganz Israel wohnten in ihren Städten. Da kam der siebte Monat heran. Die Söhne Israels waren schon in ihren Städten.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.