< Job 36 >

1 Elihu fuhr nun weiter fort:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 "Ein wenig warte noch, daß ich dich unterweise! Denn noch spricht manches auch für Gott.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Ich muß nur meinen Vortrag weiter ausdehnen; doch werde ich mein Tun rechtfertigen.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Denn nimmer sollen meine Worte dich enttäuschen, die ich an dich, Rechthaber, richte.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Sieh, Gott ist fest und widerspricht sich nicht; er ist durchaus von festem Sinn.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Er schenkt dem Frevler nicht das Leben; dem Armen aber gibt er Recht.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Von Frommen zieht er nicht die Augen ab; sogar mit Königen läßt er auf dem Thron sie sitzen, in Pracht und Herrlichkeit, und werden sie dann stolz,
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 so legt man sie in Ketten, und sie werden so gefesselt in des Elends Stricken.
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Dann hält er ihnen vor ihr Treiben, ihre Sünden, daß sie stolz geworden.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Und so tut er ihr Ohr der Warnung auf und heißt sie umkehren von Sünden.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Gehorchen sie in Unterwürfigkeit, dann fließen ihre Tage in Glückseligkeit, in Wonne ihre Jahre hin.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Doch wenn sie nicht gehorchen, rennen sie ins Dunkle und sie sterben in Verblendung.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Ruchlose Leute aber wecken Zorn und rufen nicht um Hilfe, wenn er sie fesselt.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Hin stirbt so in der Jugendfrische ihre Seele, ihr Leben in der Vollkraft.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 In seinem Elend rettet er den Armen, dieweil er in der Not ihr Ohr eröffnet.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Er lockt auch dich aus der Bedrängnis Rachen. An ihre Stelle träte Freiheit, unbeengt, und deines Tisches Schüssel würde voll von Fett.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Bist du von frevelhaftem Urteil aber voll, dann trifft auch dich gerechtes Urteil.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Denn Zorn verführe dich nicht zu dem Übermaße, der Streit um Lösung soll dich nicht verleiten.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Wird's dein Geschrei in Ordnung bringen? Unnötig sind ja all die Kraftanstrengungen.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Nicht wünsche dir die Nacht herbei! An ihre Stelle treten Unruhen.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Nimm dich in acht und kehre nimmer dich dem Frevel zu! Du hast dazu mehr Lust als zu dem Leiden.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Sieh, Gott ist groß in seiner Macht. Wer ist ein Lehrer gleich wie er?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Wer stellt ihn über seinen Weg zur Rede? Wer sagt nur: 'Du hast schlecht gehandelt'?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Bedenk, daß du sein Tun des Irrtums zeihst, das andere in Lobliedern besingen!
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Und alle Menschen haben ihre Lust daran; die Sterblichen betrachten es seit fernsten Zeiten.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Sieh, Gott ist alt, weit über unsere Begriffe, und unerforschlich seiner Jahre Zahl.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Er zählt die Wassertropfen ab, daß sie in seinen Nebel hin als Regen sickern,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 den Wolken rieseln lassen, auf viele Menschen niederträufelnd.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Wer vollends hätte Einsicht in der Wolken Weite, in das Gedröhne seines Wohngezeltes,
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 wenn er darin sein Rollen weithin tönen läßt und dann des Meeres Quellen niederrinnen?
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Denn damit gibt er Völkern Nahrung, stellt Speise her in großer Menge.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Er birgt den Blitzstrahl in den Händen, befiehlt ihm, wo er einzuschlagen hat.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Er zeigt ihm seinen Freund; den Frevler aber läßt er ihn durchbohren."
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >