< Job 12 >

1 Darauf gab Job zur Antwort:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 "Wahrhaftig, ihr seid Leute; ausstirbt mit euch die Weisheit.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Ich habe aber auch Verstand wie euer einer, ich falle gegen euch nicht ab. Wem wären solche Dinge fremd? -
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Dem Nächsten diene ich zum Schimpf, dem, der zu Gott ruft und den er erhört, dem vollkommenen Gerechten, zum Gespött.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Ich gleiche einer Nessel, gar verachtenswert, nach Ansicht Glücklicher für Fußtritte ausersehen.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Den Räubern aber sind die Zelte sicher, und Sicherheit genießen, die Gott reizen für das, was Gott in ihreHände hat gegeben.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Befrage nur die Tiere! Sie können es dir sagen; die Vögel auch beweisen dir's.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Schau dir die Erde an! Sie lehrt es dich; die Fische in dem Meer bezeugen dir's:
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Wer nur in aller Welt weiß nicht, daß Gottes Hand dies hat geschaffen,
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 daß jedes Wesen ist in seiner Hand, der Odem aller Sterblichen? -
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Ist nicht das Ohr zum Worteprüfen so geschaffen, gerade wie der Gaumen, daß er Speise koste? -
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Ist Weisheit bei den Alten, Verstand bei langem Leben bloß zu finden,
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 dann muß bei ihm recht große Weisheit, Verstand und kluger Rat zu finden sein.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Was er zerstört, das baut man nimmer auf, und nimmt er jemanden gefangen, der wird nicht wieder frei.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Wenn er den Wassern wehrt, dann bleiben sie an Ort und Stelle; wenn er sie ledig läßt, aufwühlen sie die Erde.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Von ihm kommt Stärke und Erfolg; sein ist der Irrende, sein der Verführer.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Er, der da Räte barfuß ziehen läßt und Richtern den Verstand wegnimmt,
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 der Königen die Diademe löst und ihnen Stricke um die Hüften legt,
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 der Priester barfuß ziehen läßt und der Beamte stürzt,
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 der stocken macht geübte Redner und Greisen den Verstand wegnimmt,
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 der Schande ausgießt über Vornehme und Höflingen die Schärpen lockert,
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 der Tiefes aus dem Dunkel zieht und an das Licht das Finstere bringt,
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 der Heiden in die Irre führt und sie vernichtet und Heidenvölker niederstreckt und liegen läßt,
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 der zagen macht die Landeshäupter und sie in auswegloser Wirrnis irreführt,
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 daß sie in finsterem Dunkel tappen und der sie wie Betrunkene taumeln macht."
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >