< Psalm 25 >

1 Von David. Zu dir, Jehova, erhebe ich meine Seele.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Mein Gott, auf dich vertraue ich: Laß mich nicht beschämt werden, laß meine Feinde nicht über mich frohlocken!
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Auch werden alle, die auf dich harren, nicht beschämt werden; es werden beschämt werden, die treulos handeln ohne Ursache.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Deine Wege, Jehova, tue mir kund, deine Pfade lehre mich!
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Leite mich in deiner Wahrheit und lehre mich, denn du bist der Gott meines Heils; auf dich harre ich den ganzen Tag.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Gedenke deiner Erbarmungen, Jehova, und deiner Gütigkeiten; denn von Ewigkeit her sind sie.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Gedenke nicht der Sünden meiner Jugend, noch meiner Übertretungen; gedenke du meiner nach deiner Huld, um deiner Güte willen, Jehova!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Gütig und gerade ist Jehova, darum unterweist er die Sünder in dem Wege;
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Er leitet die Sanftmütigen im Recht, und lehrt die Sanftmütigen seinen Weg.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Alle Pfade Jehovas sind Güte und Wahrheit für die, welche seinen Bund und seine Zeugnisse bewahren.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Um deines Namens willen, Jehova, wirst du ja vergeben meine Ungerechtigkeit; denn sie ist groß.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Wer ist nun der Mann, der Jehova fürchtet? Er wird ihn unterweisen in dem Wege, den er wählen soll.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Seine Seele wird im Guten wohnen, und sein Same die Erde besitzen.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Das Geheimnis Jehovas ist für die, welche ihn fürchten, und sein Bund, um ihnen denselben kundzutun.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Meine Augen sind stets auf Jehova gerichtet; denn er wird meine Füße herausführen aus dem Netze.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Wende dich zu mir und sei mir gnädig, denn einsam und elend bin ich.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Die Ängste meines Herzens haben sich vermehrt; führe mich heraus aus meinen Drangsalen!
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Sieh an mein Elend und meine Mühsal, und vergib alle meine Sünden!
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Sieh an meine Feinde, denn ihrer sind viele, und mit grausamem Hasse hassen sie mich.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Bewahre meine Seele und errette mich! Laß mich nicht beschämt werden, denn ich traue auf dich.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Lauterkeit und Geradheit mögen mich behüten, denn ich harre auf dich.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Erlöse Israel, o Gott, aus allen seinen Bedrängnissen!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Psalm 25 >