< Psalm 126 >

1 Ein Stufenlied. Als Jehova die Gefangenen Zions zurückführte, waren wir wie Träumende.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Da ward unser Mund voll Lachens, und unsere Zunge voll Jubels; da sagte man unter den Nationen: Jehova hat Großes an ihnen getan!
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 Jehova hat Großes an uns getan: wir waren fröhlich!
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Führe unsere Gefangenen zurück, Jehova, gleich Bächen im Mittagslande!
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Die mit Tränen säen, werden mit Jubel ernten.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Er geht hin unter Weinen und trägt den Samen zur Aussaat; er kommt heim mit Jubel und trägt seine Garben.
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psalm 126 >