< Psalm 114 >

1 Als Israel aus Ägypten zog, das Haus Jakob aus dem Volke fremder Sprache,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 da war Juda sein Heiligtum, Israel seine Herrschaft.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Das Meer sah es und floh, der Jordan wandte sich zurück;
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 die Berge hüpften wie Widder, die Hügel wie junge Schafe.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Was war dir, du Meer, daß du flohest? Du Jordan, daß du dich zurückwandtest?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Ihr Berge, daß ihr hüpftet wie Widder? ihr Hügel, wie junge Schafe?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Erbebe vor dem Herrn, du Erde, vor dem Gott Jakobs,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Der den Felsen verwandelte in einen Wasserteich, den Kieselfelsen in einen Wasserquell!
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalm 114 >