< Sprueche 6 >

1 Mein Sohn, wenn du Bürge geworden bist für deinen Nächsten, für einen anderen deine Hand eingeschlagen hast;
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 bist du verstrickt durch die Worte deines Mundes, gefangen durch die Worte deines Mundes:
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 tue denn dieses, mein Sohn, und reiße dich los, da du in deines Nächsten Hand gekommen bist; geh hin, wirf dich nieder, und bestürme deinen Nächsten;
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 gestatte deinen Augen keinen Schlaf, und keinen Schlummer deinen Wimpern;
Usagone tulo, usawodzere.
5 reiße dich los wie eine Gazelle aus der Hand, und wie ein Vogel aus der Hand des Vogelstellers.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Geh hin zur Ameise, du Fauler, sieh ihre Wege und werde weise.
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Sie, die keinen Richter, Vorsteher und Gebieter hat,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 sie bereitet im Sommer ihr Brot, hat in der Ernte ihre Nahrung eingesammelt.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Bis wann willst du liegen, du Fauler? Wann willst du von deinem Schlafe aufstehen?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Ein wenig Schlaf, ein wenig Schlummer, ein wenig Händefalten, um auszuruhen:
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 und deine Armut wird kommen wie ein rüstig Zuschreitender, und deine Not wie ein gewappneter Mann.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Ein Belialsmensch, ein heilloser Mann ist, wer umhergeht mit Verkehrtheit des Mundes,
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 mit seinen Augen zwinkt, mit seinen Füßen scharrt, mit seinen Fingern deutet.
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Verkehrtheiten sind in seinem Herzen; er schmiedet Böses zu aller Zeit, streut Zwietracht aus.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Darum wird plötzlich sein Verderben kommen; im Augenblick wird er zerschmettert werden ohne Heilung. -
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Sechs sind es, die Jehova haßt, und sieben sind seiner Seele ein Greuel:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Hohe Augen, eine Lügenzunge, und Hände, die unschuldiges Blut vergießen;
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 ein Herz, welches heillose Anschläge schmiedet, Füße, die eilends zum Bösen hinlaufen;
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 wer Lügen ausspricht als falscher Zeuge, und wer Zwietracht ausstreut zwischen Brüdern.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Mein Sohn, bewahre das Gebot deines Vaters, und verlaß nicht die Belehrung deiner Mutter;
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 binde sie stets auf dein Herz, knüpfe sie um deinen Hals.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Wenn du einhergehst, wird sie dich leiten; wenn du dich niederlegst, wird sie über dich wachen; und erwachst du, so wird sie mit dir reden.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Denn das Gebot ist eine Leuchte, und die Belehrung ein Licht; und die Zurechtweisung der Zucht sind der Weg des Lebens:
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 um dich zu bewahren vor dem bösen Weibe, vor der Glätte der Zunge einer Fremden.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Begehre nicht in deinem Herzen nach ihrer Schönheit, und sie fange dich nicht mit ihren Wimpern!
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 Denn um eines hurerischen Weibes willen kommt man bis auf einen Laib Brot, und eines Mannes Weib stellt einer kostbaren Seele nach. -
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Sollte jemand Feuer in seinen Busen nehmen, ohne daß seine Kleider verbrennten?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Oder sollte jemand über glühende Kohlen gehen, ohne daß seine Füße versengt würden?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 So der, welcher zu dem Weibe seines Nächsten eingeht: keiner, der sie berührt, wird für schuldlos gehalten werden. -
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Man verachtet den Dieb nicht, wenn er stiehlt, um seine Gier zu stillen, weil ihn hungert;
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 und wenn er gefunden wird, kann er siebenfach erstatten, kann alles Gut seines Hauses hingeben.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Wer mit einem Weibe Ehebruch begeht, ist unsinnig; wer seine Seele verderben will, der tut solches.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Plage und Schande wird er finden, und seine Schmach wird nicht ausgelöscht werden.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 Denn Eifersucht ist eines Mannes Grimm, und am Tage der Rache schont er nicht.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Er nimmt keine Rücksicht auf irgendwelche Sühne und willigt nicht ein, magst du auch das Geschenk vergrößern.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Sprueche 6 >