< 1 Chronik 25 >

1 Und David und die Obersten des Heeres sonderten von den Söhnen Asaphs und Hemans und Jeduthuns solche zum Dienste ab, welche weissagten mit Lauten und Harfen und mit Zimbeln. Und es war ihre Zahl, der Männer, die tätig waren für ihren Dienst:
Davide ndi atsogoleri a asilikali anapatula ena mwa ana a Asafu, Hemani ndi Yedutuni ku utumiki wa uneneri pogwiritsa ntchito apangwe, azeze ndi ziwaya zamalipenga. Tsopano nawu mndandanda wa anthu amene ankagwira ntchito imeneyi:
2 Von den Söhnen Asaphs: Sakkur und Joseph und Nethanja und Ascharela, die Söhne Asaphs, unter der Leitung Asaphs, welcher nach der Anweisung des Königs weissagte.
Kuchokera kwa ana a Asafu: Zakuri, Yosefe, Netaniya ndi Asareli. Ana a Asafu amalamulidwa ndi Asafu ndipo amanenera moyangʼaniridwa ndi mfumu.
3 Von Jeduthun, die Söhne Jeduthuns: Gedalja und Zeri und Jesaja, Haschabja und Mattithja, und Simei, sechs, unter der Leitung ihres Vaters Jeduthun, mit der Laute, welcher weissagte, um Jehova zu preisen und zu loben.
Kwa Yedutuni, kuchokera kwa ana ake: Gedaliya, Zeri, Yesaya, Simei, Hasabiya ndi Matitiya. Onse analipo 9 ndipo amayangʼaniridwa ndi Yedutuni abambo awo, amene amanenera pogwiritsa ntchito apangwe poyamika ndi kutamanda Yehova.
4 Von Heman, die Söhne Hemans: Bukkija und Mattanja, Ussiel, Schebuel und Jerimoth, Hananja, Hanani, Eliatha, Giddalti und Romamti-Eser, Joschbekascha, Mallothi, Hothir, Machasioth.
Kwa Hemani, kuchokera kwa ana ake: Bukiya, Mataniya, Uzieli, Subaeli ndi Yerimoti; Hananiya, Hanani, Eliata, Gidaliti ndi Romamiti-Ezeri; Yosibakasa, Maloti, Hotiri ndi Mahazioti.
5 Alle diese waren Söhne Hemans, des Sehers des Königs in den Worten Gottes, um seine Macht zu erheben; und Gott hatte dem Heman vierzehn Söhne und drei Töchter gegeben. -
Onsewa anali ana a Hemani mlosi wa mfumu. Iye anapatsidwa anawa potsata mawu a Mulungu akuti adzamukweza. Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna 14 ndi ana aakazi atatu.
6 Alle diese waren unter der Leitung ihrer Väter, Asaph und Jeduthun und Heman, beim Gesange im Hause Jehovas, mit Zimbeln, Harfen und Lauten, zum Dienste des Hauses Gottes, nach der Anweisung des Königs.
Anthu onsewa ankayangʼaniridwa ndi makolo awo pa mayimbidwe a mʼNyumba ya Yehova. Iwowatu ankayimba ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe potumikira mʼNyumba ya Mulungu. Koma Asafu, Yedutuni ndi Hemani amayangʼaniridwa ndi mfumu.
7 Und es war ihre Zahl mit ihren Brüdern, die im Gesange Jehovas geübt waren: aller Kundigen zweihundertachtundachtzig.
Iwo pamodzi ndi abale awo onse ophunzitsidwa ndi aluso loyimbira Yehova chiwerengero chawo chinali 288.
8 Und sie warfen Lose über ihr Amt, der Kleine wie der Große, der Kundige mit dem Lehrling.
Angʼonoangʼono ndi akulu omwe, mphunzitsi ndi wophunzira yemwe anachita maere pa ntchito zawo.
9 Und das erste Los kam heraus für Asaph, für Joseph; für Gedalja das zweite: er und seine Brüder und seine Söhne waren zwölf;
Maere woyamba amene anali a Asafu, anagwera Yosefe, ana ndi abale ake. 12 Maere achiwiri anagwera Gedaliya, ndi abale ake ndi ana ake. 12
10 das dritte für Sakkur: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achitatu anagwera Zakuri, ana ake ndi abale ake. 12
11 das vierte für Jizri: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achinayi anagwera Iziri, ana ake ndi abale ake. 12
12 das fünfte für Nathanja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achisanu anagwera Netaniya, ana ake ndi abale ake. 12
13 das sechste für Bukkija: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera Bukiya, ana ake ndi abale ake. 12
14 das siebte für Jescharela: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera Yesarela, ana ake ndi abale ake. 12
15 das achte für Jesaja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achisanu ndi chitatu anagwera Yeshaya, ana ake ndi abale ake. 12
16 das neunte für Mattanja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere achisanu ndi chinayi anagwera Mataniya, ana ake ndi abale ake. 12
17 das zehnte für Simei: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a khumi anagwera Simei, ana ake ndi abale ake. 12
18 das elfte für Asarel: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 11 anagwera Azareli, ana ake ndi abale ake. 12
19 das zwölfte für Haschabja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 12 anagwera Hasabiya, ana ake ndi abale ake. 12
20 das dreizehnte für Schubael: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 13 anagwera Subaeli, ana ake ndi abale ake. 12
21 das vierzehnte für Mattithja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 14 anagwera Matitiya, ana ake ndi abale ake. 12
22 das fünfzehnte für Jeremoth: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 15 anagwera Yeremoti, ana ake ndi abale ake. 12
23 das sechzehnte für Hananja: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 16 anagwera Hananiya, ana ake ndi abale ake. 12
24 das siebzehnte für Joschbekascha: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 17 anagwera Yosibakasa, ana ake ndi abale ake. 12
25 das achtzehnte für Hanani: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 18 anagwera Hanani, ana ake ndi abale ake. 12
26 das neunzehnte für Mallothi: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 19 anagwera Maloti, ana ake ndi abale ake. 12
27 das zwanzigste für Eliatha: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 20 anagwera Eliyata, ana ake ndi abale ake. 12
28 das einundzwanzigste für Hothir: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 21 anagwera Hotiri, ana ake ndi abale ake. 12
29 das zweiundzwanzigste für Giddalti: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 22 anagwera Gidaliti, ana ake ndi abale ake. 12
30 das dreiundzwanzigste für Machasioth: seine Söhne und seine Brüder, zwölf;
Maere a 23 anagwera Mahazioti, ana ake ndi abale ake. 12
31 das vierundzwanzigste für Romamti-Eser: seine Söhne und seine Brüder, zwölf.
Maere a 24 anagwera Romamiti-Ezeri, ana ake ndi abale ake 12.

< 1 Chronik 25 >