< 1 Chronik 24 >

1 Und was die Söhne Aarons betrifft, so waren ihre Abteilungen: Die Söhne Aarons: Nadab und Abihu, Eleasar und Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Und Nadab und Abihu starben vor ihrem Vater, und sie hatten keine Söhne; und Eleasar und Ithamar übten den Priesterdienst aus.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Und David, und Zadok von den Söhnen Eleasars, und Ahimelech von den Söhnen Ithamars teilten sie ab nach ihrem Amte, in ihrem Dienste.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Und von den Söhnen Eleasars wurden mehr Familienhäupter gefunden, als von den Söhnen Ithamars; und so teilten sie sie so ab: Von den Söhnen Eleasars sechzehn Häupter von Vaterhäusern, und von den Söhnen Ithamars acht Häupter von ihren Vaterhäusern.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Und zwar teilten sie sie durch Lose ab, diese wie jene; denn die Obersten des Heiligtums und die Obersten Gottes waren aus den Söhnen Eleasars und aus den Söhnen Ithamars.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Und Schemaja, der Sohn Nethaneels, der Schreiber aus Levi, schrieb sie auf in Gegenwart des Königs und der Obersten und Zadoks, des Priesters, und Ahimelechs, des Sohnes Abjathars, und der Häupter der Väter der Priester und der Leviten. Je ein Vaterhaus wurde ausgelost für Eleasar, und je eines wurde ausgelost für Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Und das erste Los kam heraus für Jehojarib, für Jedaja das zweite,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 für Harim das dritte, für Seorim das vierte,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 für Malkija das fünfte, für Mijamin das sechste,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 für Hakkoz das siebte, für Abija das achte,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 für Jeschua das neunte, für Schekanja das zehnte,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 für Eljaschib das elfte, für Jakim das zwölfte,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 für Huppa das dreizehnte, für Jeschebab das vierzehnte,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 für Bilga das fünfzehnte, für Immer das sechzehnte,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 für Hesir das siebzehnte, für Happizez das achtzehnte,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 für Pethachja das neunzehnte, für Jecheskel das zwanzigste,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 für Jakin das einundzwanzigste, für Gamul das zweiundzwanzigste,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 für Delaja das dreiundzwanzigste, für Maasja das vierundzwanzigste.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Das war ihre Einteilung zu ihrem Dienst, um in das Haus Jehovas zu kommen nach ihrer Vorschrift, gegeben durch ihren Vater Aaron, so wie Jehova, der Gott Israels, ihm geboten hatte.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Und was die übrigen Söhne Levis betrifft: von den Söhnen Amrams: Schubael; von den Söhnen Schubaels: Jechdeja. -
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Von Rechabja, von den Söhnen Rechabjas: das Haupt, Jischija. -
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Von den Jizharitern: Schelomoth; von den Söhnen Schelomoths: Jachath. -
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 Und die Söhne Hebrons: Jerija, das Haupt; Amarja, der zweite; Jachasiel, der dritte; Jekamam, der vierte. -
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 die Söhne Ussiels: Micha; von den Söhnen Michas: Schamir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Der Bruder Michas war Jischija; von den Söhnen Jischijas: Sekarja. -
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Die Söhne Meraris: Machli und Musi. Die Söhne Jaasijas, seines Sohnes:
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 die Söhne Meraris von Jaasija, seinem Sohne: Schoham und Sakkur und Ibri;
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 von Machli: Eleasar, der hatte aber keine Söhne;
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 von Kis, die Söhne Kis': Jerachmeel;
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 und die Söhne Musis: Machil und Eder und Jerimoth. Das waren die Söhne der Leviten, nach ihren Vaterhäusern.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Und auch sie warfen Lose wie ihre Brüder, die Söhne Aarons, in Gegenwart des Königs David und Zadoks und Ahimelechs und der Häupter der Väter der Priester und der Leviten, das Haupt der Väter wie sein geringster Bruder.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronik 24 >