< Job 34 >

1 Und Elihu hob wieder an und sprach:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Höret, ihr Weisen, meine Worte, und ihr Kundigen, gebet mir Gehör!
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Denn das Ohr prüft die Worte, wie der Gaumen die Speise kostet. [Eig. speisend kostet]
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Erwählen wir für uns, was recht, erkennen wir unter uns, was gut ist!
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Denn Hiob hat gesagt: Ich bin gerecht, und Gott [El] hat mir mein Recht entzogen.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Trotz meines Rechtes soll ich lügen; meine Wunde [Eig. mein Pfeil; vergl. Kap. 6,4;16,13] ist unheilbar, ohne daß ich übertreten habe. -
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Wer ist ein Mann wie Hiob, der Hohn trinkt wie Wasser,
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 und in Gesellschaft geht mit denen, die Frevel tun, und wandelt mit gottlosen Menschen?
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Denn er hat gesagt: Keinen Nutzen hat ein Mann davon, daß er Wohlgefallen an Gott hat! [Eig. gern mit Gott verkehrt]
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Darum höret mir zu, ihr Männer von Verstand! Fern sei Gott von Gesetzlosigkeit, und der Allmächtige von Unrecht!
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Sondern des Menschen Tun vergilt er ihm, und nach jemandes Wege läßt er es ihn finden.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Ja, wahrlich, Gott [El] handelt nicht gesetzlos, und der Allmächtige beugt nicht das Recht.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Wer hat ihm die Erde anvertraut? Und wer den ganzen Erdkreis gegründet? [Eig. gesetzt]
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Wenn er sein Herz nur auf sich selbst richtete, seinen Geist [O. Hauch] und seinen Odem an sich zurückzöge,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 so würde alles Fleisch insgesamt verscheiden, und der Mensch zum Staube zurückkehren.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Und wenn du doch dieses einsehen und hören, der Stimme meiner Worte Gehör schenken wolltest!
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Sollte auch herrschen, wer das Recht haßt? oder willst du den Allgerechten [W. den Gerecht-Mächtigen] verdammen?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Sagt man zu einem Könige: Belial, [Nichtswürdiger] zu Edlen: Du Gottloser? -
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Wieviel weniger zu ihm, der die Person der Fürsten nicht ansieht und den Reichen [O. Vornehmen] nicht vor dem Armen berücksichtigt! Denn sie alle sind das Werk seiner Hände.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 In einem Augenblick sterben sie; und in der Mitte der Nacht wird ein Volk erschüttert und vergeht, und Mächtige werden beseitigt ohne Hand. [Eig. nicht durch Hand [d. h. Menschenhand]]
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 Denn seine Augen sind auf die Wege des Menschen gerichtet, und er sieht alle seine Schritte.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Da ist keine Finsternis und kein Todesschatten, daß sich darein verbergen könnten, die Frevel tun.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Denn er braucht nicht lange auf einen Menschen acht zu geben, damit er vor Gott [El] ins Gericht komme.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Er zerschmettert Gewaltige ohne Untersuchung, und setzt andere an ihre Stelle.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Daher kennt er ihre Handlungen, und kehrt sie um über Nacht; und sie werden zermalmt.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Er schlägt sie, wie Übeltäter, auf öffentlichem Platze,
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 darum daß sie von seiner Nachfolge [Eig. von hinter ihm] abgewichen sind [And. üb.: denn darum sind sie usw.] und alle seine Wege nicht bedacht haben,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 um zu ihm hinaufdringen zu lassen das Schreien des Armen, und damit er das Schreien der Elenden höre.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Schafft er Ruhe, wer will beunruhigen? Und verbirgt er das Angesicht, wer kann ihn schauen? So handelt er sowohl gegen ein Volk, als auch gegen einen Menschen zumal,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 damit der ruchlose Mensch nicht regiere, damit sie nicht Fallstricke des Volkes seien.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Denn hat er wohl zu Gott [El] gesagt: Ich trage meine Strafe, ich will nicht mehr verderbt handeln;
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 was ich nicht sehe, zeige du mir; wenn ich Unrecht verübt habe, so will ich es nicht mehr tun? -
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Soll nach deinem Sinne er es vergelten? Denn du hast seine Vergeltung verworfen, und so mußt du wählen, [W. denn du hast verworfen, denn du mußt wählen] und nicht ich; was du weißt, reden denn!
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Männer von Verstand werden zu mir sagen, und ein weiser Mann, der mir zuhört:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 Hiob redet nicht mit Erkenntnis, und seine Worte sind ohne Einsicht.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Ach, daß doch Hiob fort und fort geprüft würde wegen seiner Antworten nach Frevlerart!
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Denn er fügt seiner Sünde Übertretung [O. Vermessenheit] hinzu, klatscht unter uns in die Hände und mehrt seine Worte gegen Gott. [El]
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >