< Job 12 >

1 Und Hiob antwortete und sprach:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Fürwahr, ihr seid die Leute, und mit euch wird die Weisheit aussterben!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Auch ich habe Verstand wie ihr; ich stehe nicht hinter euch zurück; [Eig. ich falle nicht gegen euch ab; so auch Kap. 13,2] und wer wüßte nicht dergleichen?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Ich muß einer sein, der seinem Freunde zum Gespött ist, der zu Gott ruft, und er antwortet [O. rief antwortete] ihm; der Gerechte, Vollkommene ist zum Gespött!
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Dem Unglück gebührt Verachtung nach den Gedanken des Sorglosen; sie ist bereit für die, welche mit dem Fuße wanken.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Die Zelte der Verwüster sind in Ruhe, und Sicherheit ist für die, welche Gott [El] reizen, für den, welcher Gott in seiner Hand führt. [d. h. welcher nur auf seine Hand vertraut. Vergl. Hab. 1,11]
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Aber frage doch das Vieh, und es wirds dich lehren; und das Gevögel des Himmels, und es wirds dir kundtun;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 oder rede zu der Erde, und sie wirds dich lehren; und die Fische des Meeres werden es dir erzählen.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Wer erkennte nicht an diesen allen, daß die Hand Jehovas solches gemacht hat,
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 in dessen Hand die Seele alles Lebendigen ist und der Geist alles menschlichen Fleisches?
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Soll nicht das Ohr die Worte prüfen, wie der Gaumen für sich die Speise kostet?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Bei Greisen ist Weisheit, und Einsicht bei hohem Alter.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Bei ihm ist Weisheit und Macht, sein ist Rat und Einsicht.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Siehe, er reißt nieder, und es wird nicht wieder gebaut; er schließt über jemand zu, und es wird nicht aufgetan.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Siehe, er hemmt die Wasser, und sie vertrocknen; und er läßt sie los, und sie kehren das Land um.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Bei ihm ist Kraft und vollkommenes Wissen; sein ist der Irrende und der Irreführende.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Er führt Räte beraubt [Eig. ausgezogen] hinweg, und Richter macht er zu Narren.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Die Herrschaft der Könige löst er auf, und schlingt eine Fessel [Eig. einen Gurt, ein Band] um ihre Lenden.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Er führt Priester beraubt [Eig. ausgezogen] hinweg, und Feststehende stürzt er um.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Zuverlässigen [d. h. solchen, auf deren Rat man sich verlassen kann] entzieht er die Sprache, und Alten benimmt er das Urteil.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Verachtung schüttet er auf Edle, und den Gürtel der Starken macht er schlaff.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Er enthüllt Tiefes aus der Finsternis, und Todesschatten zieht er an das Licht hervor.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Er vergrößert Nationen, und er vernichtet sie; er breitet Nationen aus, und er führt sie hinweg.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Er entzieht den Verstand den Häuptern der Völker der Erde, und macht sie umherirren in pfadloser Einöde;
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 sie tappen in der Finsternis, wo kein Licht ist, und er macht sie umherirren gleich einem Trunkenen.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >