< Psalm 106 >

1 Lobet Jah! / Danket Jahwe, denn er ist gütig; / Ewig währet ja seine Huld.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Wer kann gebührend von Jahwes Taten reden / Und all seinen Ruhm erschöpfend verkünden?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Heil denen, die das Gesetz befolgen, / Die Gerechtigkeit üben zu jeder Zeit!
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Gedenke mein, o Jahwe! / Auch mir schenk die Huld, die dein Volk erfährt! / Auch mich sieh an, wenn du ihm hilfst!
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Dann schau ich mit Lust deiner Erwählten Glück, / Dann teil ich die Freude deines Volks / Und darf mich rühmen mit deinem Erbe.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Wir haben gesündigt gleich unsern Vätern, / Haben gottlos gehandelt, gefrevelt.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Unsre Väter in Ägypten achteten nicht deiner Wunder, / Gedachten nicht deiner Gnadenfülle, / Sondern waren widerspenstig am Meer, am Schilfmeer.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Er aber rettete sie um seines Namens willen, / Um seine Macht zu beweisen.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Er schalt das Schilfmeer, da ward es trocken. / In den Fluten ließ er sie ziehn wie auf blachem Feld.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 So befreite er sie aus des Hassers Hand / Und erlöste sie aus des Feindes Gewalt.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Die Wasser bedeckten ihre Bedränger: / Nicht einer von ihnen blieb übrig.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Da vertrauten sie auf seine Worte, / Sie sangen seinen Ruhm.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Doch schnell vergaßen sie seine Taten, / Warteten nicht, daß sein Rat sich erfülle.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Sondern lüstern wurden sie in der Wüste / Und versuchten Gott in der Öde.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Da erfüllte er wohl ihr Verlangen, / Aber dann sandte er ihnen Krankheit zu.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Sie waren auch neidisch auf Mose im Lager, / Auf Aaron, Jahwes Geweihten.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Da tat sich die Erde auf: sie verschlang Datan / Und bedeckte die Rotte Abirams.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Feuer ergriff ihre Rotte, / Die Flamme verzehrte die Frevler.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Sie machten ein Kalb am Horeb / Und beteten dann dies Gußbild an.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Ihres Gottes Herrlichkeit gaben sie hin / Für das Bild eines Stieres, der Gras frißt.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Sie hatten Gott, ihren Retter, vergessen, / Der Großes getan in Ägypten,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Wunder im Lande Hams, / Erstaunliche Dinge am Schilfmeer.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Er wollte sie schon vertilgen: / Doch da trat Mose, sein Auserwählter, vor ihm in den Riß, / Um seine Zornglut abzuwenden, / Daß er sie nicht verderbe.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Sie verschmähten das köstliche Land, / Sie trauten seiner Verheißung nicht,
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 Sondern murrten in ihren Zelten, / Gehorchten nicht Jahwes Stimme.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Da hub er auf seine Hand und schwur, / Sie niederzuschlagen in der Wüste,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 Ihre Nachkommen unter die Völker zu werfen, / Sie zu zerstreuen in die Länder.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Sie hängten sich an den Baal Peôr / Und aßen Opfer für Tote.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 So reizten sie ihn mit ihrem Tun. / Da riß unter ihnen ein Sterben ein.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Nun aber trat Pinehas auf und hielt Gericht: / Da ward der Plage Einhalt getan.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Das ward ihm gerechnet zur Gerechtigkeit / Für alle Geschlechter, für immer.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Sie erzürnten ihn weiter am Haderwasser, / Und übel ging's Mose um ihretwillen.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Denn sie hatten seinem Geist widerstrebt, / So daß ihm unbedachte Worte entfuhren.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Sie vertilgten auch nicht die Völker, / Wie ihnen Jahwe geboten hatte.
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Sondern sie ließen sich ein mit den Heiden / Und nahmen an ihrem Treiben teil:
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Sie dienten ihren Götzen, / Die wurden ihnen zum Fallstrick.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Sie opferten ihre Söhne / Und ihre Töchter den bösen Geistern.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 So vergossen sie schuldlos Blut, / Das Blut ihrer Söhne und Töchter, / Die sie opferten Kanaans Götzen, / Daß das Land durch Blutschuld entweiht ward.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 So wurden sie unrein durch ihr Tun / Und fielen von Gott durch ihr Treiben ab.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Da entbrannte Jahwes Zorn wider sein Volk, / Er fühlte Abscheu gegen sein Erbe.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Drum gab er sie in der Heiden Hand, / Daß ihre Hasser über sie herrschten.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Ihre Feinde bedrängten sie, / Sie mußten sich beugen ihrer Gewalt.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Oftmals zwar befreite er sie, / Doch in Eigensinn lehnten sie sich auf: / Drum gingen sie unter in ihrer Schuld.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Er aber sah gnädig auf ihre Not, / Als er ihr lautes Schrein vernahm.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Da gedachte er ihnen an seinen Bund / Und hatte Mitleid in großer Huld.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Er ließ sie Erbarmen finden / Bei allen, die sie ins Elend geführt.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Hilf uns, Jahwe, unser Gott, / Und sammle uns aus den Heiden! / Dann wollen wir danken deinem heiligen Namen, / Uns glücklich preisen, dich zu loben.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Gepriesen sei Jahwe, Israels Gott, / Von Ewigkeit zu Ewigkeit! / Und alles Volk spreche: / "Ja wahrlich! Lobt Jah!"
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalm 106 >