< Titosas 1 >

1 Xoossas doretidayta amanoninne tumu ayanan kallethiza tumma eratethan dichanamala Xoossa aylene Yesus Kirstosape kitetida Phawulosape.
Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
2 Iza amanoyinne eratethay kaasepe ooykidi wordotonta Goday daro wodeppe kasse ba imida medhina deyo ufaysa malakko. (aiōnios g166)
ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
3 Izi kasse gidamala nuna ashida Xoossa azazon hadara imetida sabakon ba qaala qonccisides.
Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
4 Nus kothe gidida tumu amanon ta na Titosas “Xoossa aawape nuna ashida Yesus Kiristossape kiiyatethane sarotethi nes giido.
Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
5 Ta nena qarxxesen agiday burope giigana bessiza daro mishi diza gish ne gigsanamalane ta nena azazidamala katamay dizason wossa keeththa ciimata ne doranasa.
Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
6 Cmatethan doristanayti ista bolla boroy bayndayta, isi machi azinata, nayti amanizaytane waysontayta woykko azazetiza nayta awata gideto.
Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
7 Wossa keeththa ciimay Xoossas oothana hadara ekidade gididamala iza bolla wothay bayndade gidanas beses. Hesiikka ceqetizade, gutha miishan ylotizadene mathotizade, ushanchanne izas besonta ogera go7a gididaz godi eki bizade gidanas besena.
Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
8 Hesafe bollara izi imath makiizade loo7o ootho dosizade berka bena hariizade sure as xiilone bes nagetizade gidanas beses.
Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
9 Hara asata loo7o timrten miithethzadenne he loo7o timirteza ixizayta hanqanas ba tamaridamala qalan minizade gidanas beses.
Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
10 Waysizaytine dunan xalala balethzayti daroti detes; harapekka heyti qaxaretida Ayhuda asatape ammanida asata bagatakko.
Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
11 Heytanta co77u histethi beses. Gaasoyka isti besonta oogera bes go7a demanas besonta timrte tamarson keeththa asa wursi moron detes.
Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
12 Ista Nabistappe isadey ista gish hasa7ishe “Qarxesa asay wuriso wode wordanchatane ita do7ota ganjjemane azalata” giides. f/ nabeza sunthi Epimenidese.
Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
13 He markatethay tumu hessa gish ne ista loo7etha hanqista. Hesikka ista tumma amanoy danamalasa.
Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
14 Ayhuddata haysu7e woykko tumu yooppe hakida asata azazo isti siyopetto.
kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
15 Geshatas mishi wurikka geshsha shin tuatasinne amnontaytas gidikko wurikka tunakko. Harapekka ista qohaaththaaykka wurikka tunides.
Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
16 Isti bena nu Xoosu eros getes shin ba hanotethan dikokka gidiko kadetes. Isti shunizayta, azazetontaytanne loo7o oothos besontaytakko.
Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

< Titosas 1 >