< Maatosa 3 >

1 He wode xaammqiza Yaanisay asas “salo kawotethi matida gish inte nagarappe simite” gi sabakishe Yihuda bazo biittara yidess.
Mʼmasiku amenewo, Yohane Mʼbatizi anadza nalalikira mʼchipululu cha Yudeya
2
kuti, “Tembenukani mtima chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.”
3 “Goda ogge othite, wogga oggezakka lo7othite gishe bazo biittan wasiza qaala” getetidi kasse nabe Isayasan yotetidaysi Yaanisa gishasa.
Uyu ndi amene mneneri Yesaya ananena za iye kuti, “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
4 Yanisay gamela ithikkeppe othetida mayo mayess, ba xesikka dafora gixess, izi miza qummay degera essanne bole.
Zovala za Yohane zinali zopangidwa ndi ubweya wa ngamira, ndipo amamangira lamba wachikopa mʼchiwuno mwake. Chakudya chake chinali dzombe ndi uchi wa kuthengo.
5 Yerusalameppe, kumetha Yiudappene Yordanosse shahaaththaa matan diza dere wursoppe asay wuri Yaanisakko woodhdhidi
Anthu ankapita kwa iye kuchokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndi ku madera onse a Yorodani.
6 ba nagarakka izas paxxishe Yordanosse shaafan iza kushen xaamaqetidess.
Ndipo akavomereza machimo awo ankabatizidwa mu mtsinje wa Yorodani.
7 Daro farsawetinne saduqaweti izi xamaqizaso yishin beydi Yaanisay “inteno shoshato iintte sinthara diza hanqoppe atana mala intena oni beside?”
Koma iye ataona Afarisi ndi Asaduki ambiri akubwera kumene ankabatiza, anawawuza kuti, “Ana a njoka inu! Ndani anakuchenjezani kuthawa mkwiyo umene ukubwera?
8 Iintte iintte nagrappe simidaysa besiza otho othitte.
Onetsani chipatso cha kutembenuka mtima.
9 ‘Nu away Abiramey nus dess’ gizaysan interkka intena balethopitte, ta intess Xoossi hayta shuchatappe Abirames na othi denthanas danda7es gays.
Ndipo musaganize ndi kunena mwa inu nokha kuti, ‘Tili nawo abambo athu Abrahamu.’ Ndinena kwa inu kuti Mulungu akhoza kusandutsa miyala iyi kukhala ana a Abrahamu.
10 Hekko beeyxxey qanxxanas miththata garsan gigeti utidess. Hesa gish Lo7o ayfe ayfonta mithi wuri qanxxistanane taman yegistana.
Tikukamba pano nkhwangwa yayikidwa kale pa mizu ya mitengo, ndipo mtengo umene subala chipatso chabwino udulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
11 tani marotethas hathan xamaqays haray ato shin ta iza caama tokanas besontadey, tappe adhiza minoy guyera yana, izikka Xillo Ayananine tamn intena xxamaqqana.
“Ine ndikubatizani ndi madzi kusonyeza kutembenuka mtima. Koma pambuyo panga akubwera wina amene ali ndi mphamvu kuposa ine, amene sindiyenera kunyamula nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani ndi Mzimu Woyera ndi moto.
12 kath suragiza layday iza kushen dess, izikka ba kaththa baleza piti geeshana, ba gistezakka kaththa di7en qolana, happa gidikko to7onta taman xxugana.” gidess.
Mʼdzanja lake muli chopetera ndipo adzayeretsa popunthirapo pake nadzathira tirigu wake mʼnkhokwe ndi kutentha zotsalira zonse ndi moto wosazima.”
13 He wode Yesusay Yanisan xamaqistanas Galilappe Yordanose shaafa bidess.
Pamenepo Yesu anabwera kuchokera ku Galileya kudzabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
14 Gido atin Yanisay “haysi hanena tani nenan xamaqistana besishin neni waanada taakko yayi?” gidi izara eqetidess.
Koma Yohane anayesetsa kumukanira nati, “Ndiyenera kubatizidwa ndi Inu, bwanji Inu mubwera kwa ine?”
15 Yesuusaykka “aykkoyka ba ero garki! hayssa othidi nuni xilloteth wursi polans nus beses” gidess. Yansaykka iza qofa ero gi ekidess.
Yesu anayankha kuti, “Zibatero tsopano, ndi koyenera kwa ife kuchita zimenezi kukwaniritsa chilungamo chonse.” Ndipo Yohane anavomera.
16 Yesusay xamqetidi hathappe kezida mala herakka saloy doyetin Xossa ayany woolle kafo milatidi iza bolla wodhishin beyidess.
Yesu atangobatizidwa, nthawi yomweyo potuluka mʼmadzi, kumwamba kunatsekuka ndipo taonani, Mzimu wa Mulungu anatsika ngati nkhunda natera pa Iye.
17 Saloppekka “tani izan ufa7etiza nazine ta siqiza ta nazi hayssakko” giza qalay siyetidess.
Ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa amene ndikondwera naye.”

< Maatosa 3 >