< Marqqossa 16 >

1 Sanbatay adhidappe guye Magidale Marama Yaqobe aayo Maramira Salomira issippe bidi Yesusa anha tiyanas shito shamida.
Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu.
2 Samintafe koyro galas malado wontara buro awa arshey kezida mala Yesusa dufokk buro bishin
Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda
3 “Dufoza dunappe shucha nuss ooni gendersanee?” gidi ba garsan hasa7etida.
ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”
4 Issti dhoqu gi xelishin daro gitta shuchay dufoza dunappe genderidaysa beyida.
Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale.
5 Gede dufoza giddo gelida mala issi botha mayo mayida panthi ushacha bagara utidaysa beyidi dagamida.
Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.
6 Izi qass istas “Dagamopitte inte kaqetida Nazirete Yesusa koyista, izi dendidees han deena, issti iza wothidaso hayssa beyte” gidees.
Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo.
7 Gido atin inte biidi iza kalizaytasine Phixirosas kasse intes yotida mala inteppe kasetidi izi Galila bana. Inte iza hen demana gidi istas yotitte gidees.
Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’”
8 Macashatikka malaletishene kokorishe dufappe kezi baqatida. Babida gish oonasikka aykkokka qatibeytena.
Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.
9 (note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) Samintappe koyro galas Wogga wonta maladora izi hayqoppe dendidappe guye Yesusay izippe lappun daydanth kesida Magidale Maramis koyro betides.
(note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri.
10 Izakka bada kasse izara dizayti muzotishenne yekishe dishin demada yotadus.
Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira.
11 Isti Yesusay paxa dizaysanne iza ta iza beyadis gidaysa siyidi amanibeytena.
Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.
12 Hessappe guye iza kalizaytappe namm7ati gede dere gars bishin Yesusay isstas hara ass milati betidees.
Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi.
13 Isstikka simidi hessa iza kalizaytappe atidaytas yotida. Gido atin iza kalizyti siyidi amaibeytena.
Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.
14 Hessappe guye tammane issineti kaththa madan dishin Yesusay istas qoncidees. Izi hayqoppe dendin iza beyida asati isstas yotin siyidi ammanonita agida gish isstas ammanoy bayndaysanne issta wozina mumetetha gish issta borides.
Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.
15 Isstaskka hizgidees “Gede alame wursoso biite, mishracho qaala medhetetha wursoso sabakitte.”
Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse.
16 Aamanidayne xamaqetiday atana. Amanontay gidikko pirdistana.
Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa.
17 Tana amanizayta hayti malatati kalana. Isti ta sunthan daydanthata kesana, ooratha qalankka hasa7ana.
Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano;
18 Issti shoshata ba kushera oykkana, wodhiza marzekka uyikoka issta qohena. Be kushe harganchata bolla wothi wossikko haraganchati paxana.
adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”
19 Goda Yesusay hessa yotidappe gueye pudde salo dendidi bidi Xoossa ushacan utidees.
Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu.
20 Iza kalizayti hessappe kezidi wursoson adhi adhi sabakida. Godaykka isstara oothidees. Issta timirteza ekidi oothizaytas ba yotida qalakka malata othi othi minthidees.
Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.

< Marqqossa 16 >