< Zacharie 1 >
1 Au huitième mois, en la seconde année du roi Darius, la parole du Seigneur fut adressée à Zacharie, le prophète, fils de Barachie, fils d’Addo, disant:
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 Le courroux du Seigneur a été irrité contre vos pères.
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 Et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur des armées: Revenez à moi, dit le Seigneur des armées, et je reviendrai à vous, dit le Seigneur des armées.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Ne soyez pas comme vos pères auxquels les prophètes antérieurs criaient en disant: Voici ce que dit le Seigneur des armées: Revenez de vos voies mauvaises et de vos pensées très mauvaises; et ils ne m’ont pas écouté, et ils n’ont pas fait attention à moi, dit le Seigneur.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Vos pères, où sont ils? et les prophètes, est-ce qu’ils vivront éternellement?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 Mais cependant mes paroles et mes décrets, que j’ai confiés à mes serviteurs les prophètes, est-ce qu’ils n’ont pas atteint vos pères, et est-ce qu’ils se sont convertis, et ont dit: Comme le Seigneur des armées avait résolu de nous faire selon nos voies et selon nos inventions, ainsi il a fait?
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 Le vingt-quatrième jour du onzième mois appelé Sabath, en la deuxième année du roi Darius, la parole du Seigneur fut adressée à Zacharie, le prophète, fils de Barachie, fils d’Addo, disant:
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 Je vis pendant la nuit; et voilà un homme monté sur un cheval roux, et il se tenait parmi les myrtes qui étaient dans un lieu profond; et après lui des chevaux roux, mouchetés et blancs.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 Et je dis: Qui sont ceux-ci, ô mon Seigneur? Et l’ange, qui parlait en moi, me répondit: Moi, je t’indiquerai ce que ceci signifie.
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 Et l’homme qui se tenait parmi les myrtes répondit, et dit: Ceux-ci sont ceux qu’a envoyés le Seigneur, afin qu’ils parcourent la terre.
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 Et ils répondirent à l’ange du Seigneur, qui se tenait parmi les myrtes, et dirent: Nous avons parcouru la terre, et voilà que toute la terre est habitée, et est en repos.
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Et l’ange du Seigneur reprit et dit: Seigneur des armées, jusqu’à quand n’aurez-vous point pitié de Jérusalem, et des villes de Juda contre lesquelles vous êtes irrité? C’est déjà la soixante et dixième année.
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 Et le Seigneur répondit à l’ange qui parlait en moi de bonne paroles, des paroles de consolation.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 Et l’ange qui parlait en moi me dit: Crie en disant: Voici ce que dit le Seigneur des armées: Je brûle pour Jérusalem et pour Sion d’un très grand zèle.
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 Et je suis aussi enflammé d’une très grande colère contre les nations opulentes, parce que, quand moi je n’ai été qu’un peu irrité, elles, au contraire, ont aidé au châtiment.
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 À cause de cela, voici ce que dit le Seigneur: Je reviendrai à Jérusalem avec des sentiments de miséricorde; et ma maison y sera bâtie, dit le Seigneur des armées, et le niveau sera étendu sur Jérusalem.
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Crie encore, en disant: Voici ce que dit le Seigneur des armées: Mes cités regorgeront encore de biens; le Seigneur consolera encore Sion, et il choisira encore Jérusalem.
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 Et j’ai levé mes yeux, et j’ai vu; et voilà quatre cornes.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 Et j’ai dit à l’ange qui parlait en moi: Qu’est ceci? et il me répondit: Ce sont les cornes qui ont jeté au vent Juda, Israël et Jérusalem.
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 Et le Seigneur me montra quatre ouvriers.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 Et je dis: Que viennent faire ceux-ci? Il répondit en disant: Voilà les cornes qui ont jeté au vent, homme par homme, tous les habitants de Juda, et aucun d’eux n’a levé sa tête; et ceux-ci sont venus les épouvanter, afin d’abattre les cornes des nations qui ont levé la corne contre la terre de Juda pour la disperser.
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”