< Zacharie 4 >

1 Et l’ange qui parlait en moi revint, et me réveilla comme un homme qu’on réveille de son sommeil.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 Et il me dit: Que vois-tu, toi? Et je répondis: J’ai vu, et voilà un chandelier tout d’or, et sa lampe sur son sommet, et ses sept lampes au-dessus; et sept canaux aux lampes qui étaient sur son sommet;
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 Et deux oliviers au-dessus; un à la droite de la lampe, et un à sa gauche.
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 Et je pris la parole, et je dis à l’ange qui parlait en moi: Qu’est ceci, mon Seigneur?
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 Et l’ange qui parlait en moi me répondit et me dit: Est-ce que tu ne sais pas ce que c’est? Et je dis: Non, mon Seigneur.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 Et il reprit, et s’adressa à moi, disant: Voici la parole du Seigneur à Zorobabel. Ce n’est point par une armée, ni par la force, que tu achèveras le temple, mais par mon esprit, dit le Seigneur des armées.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Qu’es-tu, grande montagne, devant Zorobabel? tu seras aplanie; il posera la pierre principale, et il ajoutera une beauté égale à sa beauté.
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 Les mains de Zorobabel ont fondé cette maison, et ses mains l’achèveront; et vous saurez que le Seigneur des armées m’a envoyé vers vous.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 Car qui a vu avec mépris les jours courts? Mais on se réjouira, et on verra le plomb à la main de Zorobabel. Ce sont là les sept yeux du Seigneur qui parcourent toute la terre.
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 Et je repris et je lui dis: Que sont ces deux oliviers à la droite du chandelier, et à sa gauche?
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 Et je repris une seconde fois, et je lui dis: Que sont ces deux branches d’oliviers qui sont auprès de deux becs d’or dans lesquels sont les canaux d’or par où coule l’huile?
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 Et il m’interpella, en disant: Est-ce que tu ne sais pas ce que c’est? Et je répondis: Non, mon Seigneur.
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 Et il dit: Ce sont les deux fils de l’huile sainte, qui assistent devant le Dominateur de toute la terre.
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”

< Zacharie 4 >