< Psaumes 99 >

1 Psaume à David (de David) lui-même.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Le Seigneur est grand dans Sion; il est élevé au-dessus de tous les peuples.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Qu’ils rendent gloire à votre grand nom, parce qu’il est terrible et saint,
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 Et que l’honneur d’un roi aime le jugement. Vous avez préparé des voies droites: jugement et justice dans Jacob, c’est vous qui les avez exercés.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Exaltez le Seigneur notre Dieu, et adorez l’escabeau de ses pieds, parce qu’il est saint.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moïse et Aaron parmi ses prêtres, et Samuel entre ceux qui invoquent son nom, Invoquaient le Seigneur, et le Seigneur les exauçait;
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 C’est du milieu d’une colonne de nuée qu’il leur parlait.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 Seigneur notre Dieu, vous les exauciez: ô Dieu, vous leur avez été propice, mais en vous vengeant de toutes leurs inventions.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Exaltez le Seigneur notre Dieu, adorez-le sur sa montagne sainte; parce qu’il est saint, le Seigneur notre Dieu.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psaumes 99 >