< Psaumes 96 >

1 Lorsqu’on bâtissait la maison, après la captivité.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Chantez au Seigneur, et bénissez son nom: annoncez de jour en jour son salut.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Annoncez parmi les nations sa gloire, au milieu de tous les peuples ses merveilles.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Parce que le Seigneur est grand, et infiniment louable; il est terrible au-dessus de tous les dieux.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Parce que tous les dieux des nations sont des démons: mais le Seigneur a fait les cieux.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 La louange et la beauté sont en sa présence: la sainteté et la magnificence dans le lieu de sa sanctification.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Apportez au Seigneur, ô familles des nations, apportez au Seigneur gloire et honneur;
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Apportez au Seigneur la gloire due à son nom. Prenez des hosties, et entrez dans ses parvis;
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Adorez le Seigneur dans son saint parvis. Que toute la terre soit ébranlée devant sa face;
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Dites parmi les nations que le Seigneur a établi son règne. Car il a affermi le globe de la terre, qui ne sera pas ébranlé: il jugera les peuples avec équité.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Que les cieux se livrent à la joie, que la terre exulte, que la mer soit agitée, et sa plénitude;
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Les champs se réjouiront, et tout ce qui est en eux. Alors exulteront tous les arbres des forêts,
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 À la face du Seigneur, parce qu’il vient; parce qu’il vient juger la terre. Il jugera le globe de la terre avec équité, et les peuples selon sa vérité.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psaumes 96 >