< Psaumes 60 >
1 Pour ceux qui seront changés, pour une inscription de titre par David lui-même, pour la doctrine, Lorsqu’il brûla la Mésopotamie de Syrie et Sobal, et que Joab, étant revenu, frappa l’Idumée dans la vallée des Salines, par la défaite de douze mille hommes. Ô Dieu, vous nous avez rejetés, et vous nous avez détruits; vous avez été irrité; et ensuite vous avez eu pitié de nous.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Vous avez ébranlé la terre, et vous l’avez bouleversée; réparez ses brisures, parce qu’elle a été ébranlée.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Vous avez montré à votre peuple des châtiments rigoureux; vous nous avez fait boire du vin de componction.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 Vous avez donné à ceux qui vous craignent un signal, afin qu’ils fuient à la face de l’arc:
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Sauvez-moi par votre droite, et exaucez-moi.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Dieu a parlé dans son sanctuaire: Je me réjouirai, et je partagerai Sichem, et je mesurerai la vallée des tabernacles.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 À moi est Galaad, et à moi est Manassé, et Ephraïm est la force de ma tête.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab est le vase de mon espérance. Jusque dans l’Idumée j’étendrai mes pas; des étrangers me sont devenus amis.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Qui me conduira dans une ville fortifiée? qui me conduira jusque dans l’Idumée?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Ne sera-ce pas vous, ô Dieu, qui nous avez rejetés? et ne sortirez-vous point, ô Dieu, à la tête de nos armées?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Donnez-nous du secours, pour nous tirer de la tribulation, parce que vain est le salut de l’homme.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 En Dieu nous ferons preuve de valeur; et lui-même réduira au néant ceux qui nous tourmentent.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.