< Psaumes 59 >
1 Ne perdez pas entièrement; par David, pour une inscription de titre, quand Saül envoya des gens et fit garder sa maison afin de le tuer (I Rois 19,11). Arrachez-moi à mes ennemis, ô mon Dieu; et délivrez-moi de ceux qui s’insurgent contre moi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Délivrez-moi de ceux qui opèrent l’iniquité; et sauvez-moi des hommes de sang.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Car voilà qu’ils ont pris mon âme; des forts ont fondu sur moi.
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Ni mon iniquité ni mon péché, Seigneur, n’en ont été cause; c’est sans iniquité que j’ai couru et que j’ai dirigé mes voies.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Levez-vous au-devant de moi, et voyez, Seigneur Dieu des armées, Dieu d’Israël.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Ils reviendront vers le soir, et ils seront affamés comme des chiens, et ils tourneront autour de la ville.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Voici qu’ils parleront dans leur bouche; et un glaive est sur leurs lèvres, en disant: Qui nous a entendus?
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Mais vous, Seigneur, vous vous rirez d’eux; vous réduirez au néant toutes les nations.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 Je garderai pour vous ma force; parce que, ô Dieu, vous êtes mon soutien.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Mon Dieu! sa miséricorde me préviendra.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Dieu me montrera le sort de mes ennemis: ne les tuez point, de peur que mon peuple n’oublie leur châtiment. Dispersez-les par votre puissance et faites-les déchoir, ô mon protecteur, ô Seigneur!
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 À cause du crime de leur bouche et du discours de leurs lèvres; et qu’ils soient pris dans leur orgueil.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 À leur consommation, à la colère de leur consommation, et ils ne seront plus.
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 Ils reviendront vers le soir, et ils seront affamés comme des chiens; et ils tourneront autour de la ville.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Ils se disperseront pour manger: mais s’ils ne sont pas rassasiés, ils murmureront.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Pour moi, je chanterai votre force; et je célébrerai dans des transports de joie, dès le matin, votre miséricorde. Parce que vous êtes devenu mon soutien et mon refuge au jour de ma tribulation.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Ô mon aide, je vous célébrerai, parce que vous êtes mon Dieu, mon soutien; mon Dieu, ma miséricorde.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.