< Psaumes 52 >
1 Pour la fin. Intelligence à David, Lorsque Doëg l’Iduméen vint annoncer à Saül que David était venu dans la maison d’Achimélech. Pourquoi te glorifies-tu en ta malice, toi qui es puissant en iniquité?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 Tout le jour, ta langue a médité l’injustice: comme un rasoir aiguisé, tu as trompé.
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
3 Tu as aimé la malice plus que la bonté; et un langage d’iniquité plutôt que d’équité.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
4 Tu as aimé toutes les paroles de perdition, ô langue trompeuse!
Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
5 C’est pour cela que Dieu te détruira pour toujours, et t’enlèvera et t’exilera, toi, de ton tabernacle, et ta racine de la terre des vivants.
Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 Les justes le verront, et ils craindront; et ils riront de lui, et diront:
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 Voilà un homme qui n’a pas pris Dieu pour son aide, mais qui a espéré dans la multitude de ses richesses, et qui s’est prévalu de sa vanité.
“Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
8 Pour moi, je suis comme un olivier qui porte du fruit dans la maison de Dieu; j’ai espéré dans la miséricorde de Dieu pour l’éternité, et pour les siècles des siècles.
Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
9 Je vous louerai pour toujours de ce que vous avez fait, et j’attendrai votre nom, parce qu’il est bon, en présence de vos saints.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.