< Psaumes 48 >

1 Psaume du cantique aux fils de Coré pour le second jour de la semaine. Le Seigneur est grand et très digne de louange, dans la cité de notre Dieu, et sur sa montagne sainte.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 La montagne de Sion est fondée à l’exultation de toute la terre; du côté de l’aquilon est la cité du grand Roi.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Dieu sera connu dans ses maisons, quand il en prendra la défense.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Car voilà que les rois de la terre se sont réunis et sont venus ensemble.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 L’ayant vu eux-mêmes, ils ont été étonnés, ils ont été troublés, ils ont été fort émus:
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Un tremblement les a saisis. Là ils ont ressenti comme les douleurs d’une femme qui enfante:
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Ainsi par un vent impétueux, vous briserez les vaisseaux de Tharsis.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Ce que nous avions appris, nous l’avons vu dans la cité du Seigneur des armées, dans la cité de notre Dieu: Dieu l’a fondée pour l’éternité.
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Nous avons reçu, ô Dieu, votre miséricorde, au milieu de votre temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Comme votre nom, ô Dieu, ainsi votre louange s’étend jusqu’aux extrémités de la terre: votre droite est pleine de justice.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Que la montagne de Sion se réjouisse, et que les filles de Juda tressaillent d’allégresse, à cause de vos jugements, Seigneur.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Environnez Sion et embrassez-la: racontez toutes ces choses dans ses tours.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Portez votre attention sur sa force: faites le dénombrement de ses maisons, afin que vous le racontiez à une autre génération.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Parce que c’est lui qui est Dieu, notre Dieu pour l’éternité et pour les siècles des siècles: lui-même qui nous gouvernera dans les siècles.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Psaumes 48 >