< Psaumes 38 >
1 Psaume de David, en souvenir touchant le sabbat. Seigneur, ne me reprenez pas dans votre fureur, et dans votre colère ne me châtiez pas.
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 Parce que j’ai été percé de vos flèches; et que vous avez appesanti sur moi votre main.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 Il n’y a rien de sain dans ma chair en présence de votre fureur: il n’y a pas de paix dans mes os en présence de mes péchés.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 Parce que mes iniquités se sont élevées au-dessus de ma tête; et comme un fardeau pesant, elles se sont appesanties sur moi.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Mes plaies se sont putréfiées et corrompues en présence de ma folie.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Je suis devenu malheureux, et je suis entièrement courbé: et tout le jour je marchais contristé.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 Parce que mes reins ont été remplis d’illusions, et qu’il n’y a rien de sain dans ma chair.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 J’ai été affligé et j’ai été humilié à l’excès; je rugissais dans le frémissement de mon cœur.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Seigneur, devant vous est tout mon désir, mon gémissement ne vous est pas caché.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Mon cœur a été troublé, ma force m’a abandonné, et la lumière de mes yeux, elle-même n’est plus avec moi.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Mes amis et mes proches se sont approchés vis-à-vis de moi, et ils se sont arrêtés. Et ceux qui étaient près de moi s’en sont tenus éloignés:
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 Et ceux qui cherchaient mon âme usaient de violence envers moi.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Mais moi, comme un sourd, je n’entendais pas; et j’étais comme un muet qui n’ouvre pas la bouche.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Je suis donc devenu comme un homme qui n’entend point, et qui n’a pas dans sa bouche de répliques.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Parce que c’est vous. Seigneur, en qui j’ai espéré: c’est vous qui m’exaucerez. Seigneur mon Dieu.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Parce que j’ai dit: Que mes ennemis ne se réjouissent jamais à mon sujet: et tandis que mes pieds étaient chancelants, ils ont parlé à mon sujet avec orgueil.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Parce que moi je suis prêt à des châtiments, et que ma douleur est toujours en ma présence.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Parce que je publierai mon iniquité; et que je penserai à mon péché.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Mais mes ennemis vivent et se sont fortifiés contre moi; et ils se sont multipliés ceux qui me haïssent injustement.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 Ceux qui me rendent des maux pour des biens me déchiraient, parce que je m’attachais au bien.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Ne m’abandonnez pas, Seigneur mon Dieu; ne vous éloignez pas de moi.
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Songez à me secourir, Seigneur, Dieu de mon salut.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.