< Psaumes 20 >

1 Pour la fin, psaume de David. Que le Seigneur vous exauce au jour de la tribulation; que le nom du Dieu de Jacob vous protège.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Qu’il vous envoie du secours du lieu saint; et que de Sion il vous défende.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Qu’il se souvienne de tous vos sacrifices, et que votre holocauste lui soit agréable.
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Qu’il vous rende selon votre cœur, et qu’il confirme tous vos desseins.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Nous nous réjouirons de votre salut; et dans le nom de notre Dieu nous nous glorifierons.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Que le Seigneur accomplisse toutes vos demandes; maintenant j’ai reconnu que le Seigneur a sauvé son Christ. Il l’exaucera du ciel, son sanctuaire: le salut de sa droite est puissant.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Ceux-ci se confient dans des chariots, et ceux-là dans des chevaux; mais nous, c’est le nom du Seigneur que nous invoquerons.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Ils ont été pris dans des lacs, et ils sont tombés; mais nous, nous nous sommes relevés et nous sommes restés debout,
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Seigneur, sauvez le roi, et exaucez-nous au jour où nous vous invoquerons.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Psaumes 20 >