< Psaumes 111 >

1 Je vous louerai, Seigneur, en tout mon cœur; en conseil des justes et en assemblée.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Grandes sont les œuvres du Seigneur; parfaitement conformes à toutes ses volontés.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Louange et magnificence est son ouvrage, et sa justice demeure dans les siècles des siècles.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Il a consacré la mémoire de ses merveilles, le Seigneur miséricordieux et compatissant;
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Il a donné une nourriture à ceux qui le craignent. Il se souviendra à jamais de son alliance,
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Il annoncera la puissance de ses œuvres à son peuple,
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Afin de leur donner l’héritage des nations: les œuvres de ses mains sont vérité et justice.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Tous ses commandements sont fidèles, confirmés dans les siècles des siècles, faits selon la vérité et l’équité.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Il a envoyé la rédemption à son peuple: il a établi pour l’éternité son alliance. Saint et terrible est son nom;
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Le commencement de la sagesse est la crainte du Seigneur. La bonne intelligence est à tous ceux qui agissent conformément à cette crainte. Sa louange demeure dans les siècles des siècles.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psaumes 111 >