< Psaumes 109 >
1 Pour la fin, psaume de David.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Dieu, ne taisez pas ma louange, parce que la bouche d’un pécheur et la bouche d’un trompeur est ouverte contre moi.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Ils ont parlé contre moi avec une langue trompeuse, et de discours de haine ils m’ont environné, et ils m’ont attaqué gratuitement.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 Au lieu de m’aimer, ils disaient du mal de moi; mais moi je priais.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Ils m’ont rendu des maux pour des biens, et de la haine pour mon amour.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Établissez sur lui un pécheur, et que le diable se tienne à sa droite.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Lorsqu’on le jugera, qu’il sorte condamné, et que sa prière même se tourne en péché.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Que ses jours soient réduits à un petit nombre, et qu’un autre reçoive son épiscopat.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Que ses fils deviennent orphelins, et sa femme, veuve.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Que ses fils ballottés soient transférés d’un lieu dans un autre, et qu’ils mendient, et qu’ils soient chassés de leurs habitations.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Qu’un usurier scrute tout ce qu’il possède, et que des étrangers ravissent le fruit de ses travaux.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Qu’il n’y ait personne qui l’assiste, et qu’il n’y ait personne qui prenne pitié de ses orphelins.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Que ses enfants soient dévoués à la mort, qu’en une seule génération son nom s’efface.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Qu’en mémoire revienne l’iniquité de ses pères, devant le Seigneur; et que le péché de sa mère ne soit point effacé.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Que ces péchés soient toujours devant le Seigneur, et que leur mémoire périsse entièrement de la terre;
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Parce qu’il ne s’est point souvenu de faire miséricorde.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Et qu’il a persécuté un homme sans ressource, mendiant et brisé de douleur.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Il a aimé la malédiction, et elle viendra à lui: il n’a pas voulu la bénédiction, et elle s’éloignera de lui. Il s’est revêtu de la malédiction comme d’un vêtement, et elle est entrée comme de l’eau dans ses entrailles, et comme de l’huile dans ses os.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Qu’elle lui soit comme le vêtement dont il se couvre, et comme la ceinture dont il est toujours ceint.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Telle est, auprès du Seigneur, l’œuvre de ceux qui parlent mal de moi, de ceux qui blasphèment contre moi.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Et vous, Seigneur, Seigneur, agissez avec moi à cause de votre nom, parce que douce est votre miséricorde. Délivrez-moi,
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Parce que moi, je suis indigent et pauvre, et que mon cœur s’est troublé au dedans de moi.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Comme l’ombre, lorsqu’elle déchue, j’ai été enlevé, et j’ai été chassé comme les sauterelles.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mes genoux ont été affaiblis par le jeûne, et ma chair a été changée à cause de l’huile qui m’a manqué.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Je suis devenu un opprobre pour eux; ils m’ont vu et ils ont secoué la tête.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Aidez-moi, Seigneur mon Dieu: sauvez-moi selon votre miséricorde.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Qu’ils sachent que votre main est là, et que c’est vous, Seigneur, qui avez fait cela.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Ils me maudiront eux, et vous, vous me bénirez: que ceux qui s’insurgent contre moi soient confondus; mais votre serviteur sera dans l’allégresse.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Qu’ils soient revêtus de honte, ceux qui disent du mal de moi: qu’ils soient couverts de leur confusion comme d’un manteau.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Je glorifierai le Seigneur de toute la puissance de ma voix, je chanterai ses louanges au milieu d’une multitude.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 Parce qu’il s’est tenu à la droite du pauvre, afin de sauver mon âme de ceux qui la persécutaient.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.