< Proverbes 6 >

1 Mon fils, si tu t’es rendu garant pour ton ami, et que tu aies engagé à un étranger ta main,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 Tu t’es enlacé par les paroles de ta bouche, et tu as été pris par tes propres discours.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Fais donc ce que je dis, mon fils, délivre-toi toi-même, parce que tu es tombé dans la main de ton prochain. Cours de tous côtés, hâte-toi, réveille ton ami;
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 N’accorde point de sommeil à tes yeux, et que tes paupières ne s’assoupissent point.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Dégage-toi, comme un petit daim qui échappe de la main, et comme un oiseau qui fuit de la main d’un oiseleur.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Va à la fourmi, ô paresseux, et considère ses voies, et apprends la sagesse;
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 La fourmi, quoiqu’elle n’ait ni chef, ni maître, ni prince,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Prépare dans l’été sa nourriture, et rassemble durant la moisson ce qu’elle doit manger.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Jusqu’à quand, paresseux, dormiras-tu? quand sortiras-tu de ton sommeil?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Tu dormiras un peu, tu sommeilleras un peu, tu mettras un peu les mains l’une dans l’autre, afin que tu dormes:
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 Et viendra à toi, comme un coureur de chemin, la détresse; et la pauvreté comme un homme armé. Mais si tu es actif, viendra ta moisson comme une source abondante, et la détresse fuira loin de toi.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Un homme apostat, homme inutile, va tenant des discours pervers,
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 Fait signe des yeux, frappe du pied, parle avec un doigt,
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Avec un cœur dépravé il machine le mal, et en tout temps il sème des querelles;
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 En un moment lui viendra sa perte, et soudain il sera brisé, et il n’aura plus de remède.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Il y a six choses que hait le Seigneur, et la septième, son âme la déteste:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Des yeux altiers, une langue menteuse, des mains versant un sang innocent,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 Un cœur formant des pensées très mauvaises, des pieds prompts à courir au mal,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 Un témoin fallacieux proférant des mensonges, et celui qui, entre des frères, sème des discordes.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Conserve, mon fils, les préceptes de ton père, et ne rejette pas la loi de ta mère.
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Lie-les dans ton cœur continuellement, et mets-les autour de ton cou.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Lorsque tu vas et viens, qu’ils marchent avec toi: lorsque tu dors, qu’ils te gardent, et te réveillant, parle avec eux;
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Parce qu’un commandement est un flambeau, et la loi, une lumière, et que c’est la voie de la vie qu’une remontrance de discipline;
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 Afin qu’ils te préservent d’une femme corrompue et de la langue flatteuse d’une étrangère.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Que ton cœur ne se passionne point pour sa beauté; et ne sois point pris par les signes de ses yeux;
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 Car le prix d’une prostituée est à peine d’un pain seul; mais une femme ravit l’âme précieuse d’un homme.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Est-ce qu’un homme peut cacher du feu dans son sein, sans que ses vêtements s’embrasent?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Ou marcher sur des charbons ardents, sans que soient brûlées les plantes de ses pieds?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 Ainsi celui qui s’approche de la femme de son prochain ne sera pas pur lorsqu’il l’aura touchée.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Ce n’est pas une grande faute, lorsque quelqu’un dérobe afin de remplir son âme affamée;
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 Pris, il rendra même le septuple, et il livrera tout ce qu’il a dans sa maison.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Mais celui qui est adultère, à cause de son manque de cœur, perdra son âme;
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Il rassemble sur lui la turpitude et l’ignominie, et son opprobre ne sera pas effacé;
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 Parce que la jalousie et la fureur du mari ne pardonneront pas au jour de la vengeance,
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Et il n’acquiescera aux prières de personne, et il ne recevra pas pour satisfaction les dons les plus nombreux.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Proverbes 6 >