< Proverbes 22 >
1 Mieux vaux une bonne renommée que beaucoup de richesses: au-dessus de l’argent et de l’or est la bonne amitié.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Le riche et le pauvre se sont rencontrés. Le créateur de l’un et de l’autre, c’est le Seigneur.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 l’homme habile a vu le mal et s’est caché: le simple a passé outre et il a souffert du dommage.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 La fin de la modestie est la crainte du Seigneur, les richesses, la gloire et la vie.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Des armes et des glaives se trouvent sur la voie du pervers; mais celui qui garde son âme s’en retire bien loin.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 C’est un proverbe: Le jeune homme suit sa voie; lors même qu’il sera vieux, il ne s’en écartera pas.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Le riche commande aux pauvres; et celui qui emprunte est l’esclave de celui qui prête.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Celui qui sème l’iniquité moissonnera des maux, et par la verge de sa colère il sera détruit.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Celui qui est porté à la miséricorde sera béni: il a donné de son pain au pauvre. Il obtiendra la victoire et l’honneur, celui qui fait des présents; mais il ravit l’âme de ceux qui les reçoivent.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Chasse le railleur, et s’en ira avec lui la querelle, et cesseront les plaintes et les outrages.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Celui qui aime la pureté du cœur, à cause de la grâce de ses lèvres, aura pour ami le roi.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Les yeux du Seigneur gardent la science; mais les paroles de l’homme inique sont confondues.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Le paresseux dit: Le lion est dehors, au milieu des rues je dois être tué.
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 C’est une fosse profonde que la bouche de l’étrangère; celui contre qui le Seigneur est irrité y tombera.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 La folie est liée au cœur de l’enfant, et la verge de la discipline la fera fuir.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Celui qui opprime le pauvre pour augmenter ses richesses donnera lui-même à un plus riche et sera dans la détresse.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Incline ton oreille, et écoute les paroles des sages; applique ton cœur à ma doctrine.
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Elle sera belle pour toi, lorsque tu la garderas au fond de ton cœur, et elle se répandra sur tes lèvres;
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Afin que ta confiance soit dans le Seigneur: c’est pour cela que je te l’ai montrée aujourd’hui,
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Voilà que je te l’ai décrite triplement, avec réflexion et science;
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Afin de te montrer la certitude et les paroles de la vérité, pour répondre à ceux qui t’ont envoyé.
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Ne fais point violence au pauvre, parce qu’il est pauvre: et ne brise pas l’indigent à la porte;
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Parce que le Seigneur jugera sa cause, et il percera ceux qui ont percé son âme.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Ne sois pas ami d’un homme colère, et ne marche pas avec un homme furieux;
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 De peur que tu n’apprennes ses voies, et que tu n’en retires un scandale pour ton âme.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Ne sois point avec ceux qui engagent leurs mains, et qui se rendent caution des dettes;
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 Car si tu n’as pas de quoi rendre, quel motif y a-t-il pour qu’il emporte la couverture de ton lit?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Ne dépasse pas les anciennes bornes qu’ont posées tes pères.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 As-tu vu un homme prompt dans son œuvre? il se tiendra devant les rois, et il ne sera pas devant les hommes obscurs.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.