< Proverbes 15 >
1 Une douce réponse brise la colère: une parole dure excite la fureur.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 La langue des sages embellit la science; la bouche des insensés fait jaillir la folie.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 En tout lieu, les yeux du Seigneur observent les bons et les méchants.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 La langue pacifique est un arbre de vie; mais celle qui est immodérée brisera l’esprit.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 L’insensé se moque de la discipline de son père; mais celui qui est docile aux réprimandes deviendra plus sage. Dans une abondante justice est une très grande vertu; mais les pensées des méchants seront déracinées.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 La maison du juste est une grande force; et dans les fruits de l’impie il n’y a que trouble.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Les lèvres des sages répandront la science: le cœur des insensés sera tout à fait différent.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Les victimes des impies sont abominables au Seigneur, les vœux des justes lui sont agréables.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 C’est une abomination pour le Seigneur, que la voie de l’impie: celui qui suit la justice est aimé de lui.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 La doctrine est odieuse à celui qui abandonne la voie de la vie; celui qui hait les réprimandes mourra.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 L’enfer et la perdition sont à nu devant le Seigneur; combien plus les cœurs des fils des hommes? (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 L’homme pernicieux n’aime pas celui qui le reprend, et ne va pas vers les sages.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Un cœur joyeux rassérène le visage; par la tristesse de l’âme, l’esprit est abattu.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Le cœur du sage cherche la doctrine; et la bouche des insensés se repaît d’ignorance.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Tous les jours du pauvre sont mauvais; l’âme tranquille est comme un continuel festin.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Mieux vaut peu avec la crainte du Seigneur que des trésors grands et inépuisables.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Mieux vaut être convié à un repas d’herbes où règne la charité, qu’à manger avec de la haine un veau engraissé.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 L’homme colère excite des querelles; celui qui est patient apaise celles qui étaient déjà suscitées.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 Le chemin des paresseux est comme une haie d’épines; la voie des justes est sans pierre d’achoppement.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Un fils sage réjouit son père; et un homme insensé méprise sa mère.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 La folie est joie pour l’insensé: et l’homme prudent dirige ses pas.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Les pensées se dissipent là où il n’y a point de conseil; mais où il y a plusieurs conseillers, elles s’affermissent.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 L’homme se réjouit de la sentence sortie de sa bouche; et la parole opportune est excellente.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Le sentier de la vie est au-dessus de l’homme instruit, afin qu’il se détourne de l’enfer le plus profond. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 Le Seigneur démolira la maison des superbes; et il affermira les bornes du champ de la veuve,
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 C’est l’abomination du Seigneur que les pensées mauvaises; mais la parole pure, très belle, sera affermie par lui.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Celui-là trouble sa maison, qui court après l’avarice; mais celui qui hait les présents vivra. Par la miséricorde et par la foi se purifient les péchés; mais c’est par la crainte du Seigneur que chacun se détourne du mal.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 L’esprit du juste médite l’obéissance: la bouche des impies déborde en mauvais discours.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 Le Seigneur est loin des impies; et il exaucera les prières des justes.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 La lumière des yeux réjouit l’âme; la bonne réputation engraisse les os.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 L’oreille qui écoute les réprimandes de vie demeurera au milieu des sages.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Celui qui rejette la discipline méprise son âme: mais celui qui acquiesce aux réprimandes a du cœur.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 La crainte du Seigneur est une discipline de sagesse; et l’humilité précède la gloire.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.