< Proverbes 1 >

1 Paraboles de Salomon, fils de David et roi d’Israël,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Utiles pour connaître la sagesse et la discipline,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Pour comprendre les paroles de la prudence, pour recevoir l’instruction de la doctrine, la justice, et le jugement et l’équité,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Afin que soit donnée aux tout petits la finesse, à l’adolescent la science et l’intelligence.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Le sage, en écoutant, sera plus sage, et l’intelligent possédera les moyens de gouverner.
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 Il découvrira le proverbe et l’interprétation, les paroles des sages et leurs énigmes.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 La crainte du Seigneur est le principe de la sagesse. La sagesse et la doctrine, les insensés les méprisent.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Écoute, mon fils, la discipline de ton père, et ne rejette pas la loi de ta mère,
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Afin que soit ajouté un agrément à ta tête, et un collier à ton cou.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Mon fils, si des pécheurs veulent l’attirer, n’y acquiesce pas.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 S’ils disent: Viens avec nous, dressons des embûches au sang, cachons des pièges à l’innocent qui ne l’a pas mérité;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Comme l’enfer, engloutissons-le vivant et entier, comme celui qui descend dans la fosse. (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Nous trouverons toutes sortes de biens précieux: nous remplirons nos maisons de dépouilles.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Mets ta part avec nous, qu’une seule bourse soit pour nous tous.
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Mon fils, ne marche pas avec eux, écarte ton pied de leurs sentiers.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Car leurs pieds courent au mal, et ils se hâtent afin de verser le sang.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Mais en vain l’on jette le filet devant les yeux des oiseaux.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Eux aussi à leur propre sang dressent des embûches, et
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Ainsi sont les sentiers de tout avare, ils ravissent lame de tous ceux qui possèdent.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La sagesse prêche dehors; dans les places publiques elle élève sa voix;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 À la tête des foules elle crie, aux portes de la ville elle profère ses paroles disant:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Jusques à quand, tout petits enfants, aimerez-vous l’enfance, et les insensés désireront-ils ce qui leur est pernicieux, et les imprudents haïront-ils la science?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Convertissez-vous à mes remontrances: voici que je vous révélerai mon esprit, et que je vous ferai comprendre mes paroles.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Parce que j’ai appelé, et que vous avez refusé de m’entendre; que j’ai tendu ma main, et qu’il n’y a eu personne qui m’ait regardé;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Que vous avez méprisé tous mes conseils, et négligé mes réprimandes:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Moi aussi, à votre mort, je rirai et je me moquerai, lorsque ce que vous craigniez vous sera arrivé.
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Lorsqu’une calamité arrivera tout d’un coup, et que la mort, comme une tempête, fondra violemment sur vous; quand, viendront sur vous la tribulation et l’angoisse:
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Alors ils m’invoqueront, et je ne les exaucerai pas; dès le matin ils se lèveront, et ils ne me trouveront pas;
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Parce qu’ils ont haï la discipline, et qu’ils n’ont pas reçu la crainte du Seigneur,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Qu’ils n’ont pas acquiescé à mes conseils, qu’ils ont déprécié toutes mes remontrances.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Aussi ils mangeront les fruits de leurs voies, et ils seront rassasiés de leurs conseils.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 L’égarement des tout petits les tuera; et la prospérité des insensés les perdra.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Mais celui qui m’écoute reposera sans terreur et jouira de l’abondance, la crainte des maux ayant été enlevée.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbes 1 >